NYIMBO 29
Tizichita Zinthu Zogwirizana Ndi Dzina Lathu
Losindikizidwa
1. Yehova Mulungu wamphamvuyonse,
Wachilungamo ndi wachikondi,
Mwini choonadi komanso nzeru,
Mukulamulira monga Mfumu.
Timasangalala potumikira
Ndi polengeza Ufumu wanu.
(KOLASI)
Tiyesetse kuchita zinthu zomwe
N’zogwirizana ndi dzina lathu.
2. Tikamatumikira ndi abale
Timakhaladi ogwirizana.
Tikaphunzitsa anthu choonadi,
Dzina lanu limatamandidwa.
Ndife odziwika ndi dzina lanu,
Tipitiriza kulitchukitsa.
(KOLASI)
Tiyesetse kuchita zinthu zomwe
N’zogwirizana ndi dzina lathu.
(Onaninso Deut. 32:4; Sal. 43:3; Dan. 2:20, 21.)