Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • ‘Ndingachitirenji Choipa Chachikulu N’kuchimwira Mulungu?’
    Nsanja ya Olonda—2014 | November 1
    • Yosefe anapewa kumangoganizira za mavuto amene ankakumana nawo ndipo ankagwira ndi mtima wonse ntchito yomwe anapatsidwa. Zimenezi zinapangitsa kuti Yehova amudalitse ndipo abwana ake anayamba kumukonda kwambiri. Potifara anaona kuti Yehova ankadalitsa kwambiri Yosefe. Ndipo n’zosakayikitsa kuti zimenezi zinapangitsa kuti zinthu ziziyenda bwino panyumba ya Potifara. Pamapeto pake Potifara anayamba kukhulupirira kwambiri Yosefe moti anasiya chilichonse m’manja mwake.—Genesis 39:3-6.

  • ‘Ndingachitirenji Choipa Chachikulu N’kuchimwira Mulungu?’
    Nsanja ya Olonda—2014 | November 1
    • Baibulo limanena kuti Yosefe anapitiriza kukula ndipo anali “wokongola m’maonekedwe ndi wa thupi loumbika bwino.” Komatu zimenezi zinamubweretsera mavuto chifukwa munthu akakhala wokongola, nthawi zambiri anthu amamusilira.

      Mkazi wa Potifara akuyang’ana Yosefe momusirira akugwira ntchito ndi akapolo ena

      Mkazi wa Potifara anayamba kusirira Yosefe

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena