-
Mulungu Akulinganiza Kuti Munthu Asangalale ndi Moyo M’paradaisoNsanja ya Olonda—1989 | August 1
-
-
9 “Ndipo Yehova Mulungu anaumba munthu ndi dothi lapansi, nawuzira mpweya wa moyo m’mphuno mwake; munthuyo nakhala wamoyo. Ndipo Yehova Mulungu anabzala m’munda ku Edene chakum’mawa; momwemo ndipo adaika munthu adamuumbayo. Ndipo Yehova Mulungu anameretsa m’nthaka mitengo yonse yokoma m’maso ndi yabwino kudya; ndiponso mtengo wa moyo pakati pa mundapo, ndi mtengo wakudziŵitsa zabwino ndi zoipa. Ndipo unatuluka m’Edene mtsinje wakuthirira m’mundamo, mmenemo ndipo unalekana nuchita miyendo inayi.”—Genesis 2:7-10.b “Dzina la wakuyamba ndi Pisoni: umenewo ndiwo wozungulira dziko lonse la Havila, mmene muli golidi; golidi wa dziko ali wabwino; ndimonso muli bedola ndi mwala wasohamu. Dzina la mtsinje wachiŵiri ndi Gihoni: umenewo ndiwo wozungulira dziko lonse la Kusi. Dzina la mtsinje wachitatu ndi Hidikeli: umenewo ndiwo wakuyenda cha kum’mawa kwake kwa Asuri. Mtsinje wachinayi ndi Firate.”—Genesis 2:11-14.
-
-
Mulungu Akulinganiza Kuti Munthu Asangalale ndi Moyo M’paradaisoNsanja ya Olonda—1989 | August 1
-
-
b Mneneri Mose, yemwe analemba chidziŵitsocho m’bukhu la Genesis m’zana la 16 Nyengo yathu Yachisawawa isadakhale, anawonjezera chidziŵitso chotsatirachi ponena za mtsinje wa mu Edene umenewu, mogwirizana ndi chidziŵitso cha m’tsiku lake:
Ndi Ati Omwe Ali Mayankho Anu?
-