-
Buku Lothandiza pa Moyo WamakonoBuku la Anthu Onse
-
-
Kusiyana ndi zimenezo, Baibulo limapereka uphungu wodalirika ndi wabwino pankhani ya ukwati. Limavomereza kuti nthaŵi zina zinthu zikafika poipa chisudzulo chimaloleka. (Mateyu 19:9) Komanso, limatsutsa kusudzulana pazifukwa zopanda kumutu. (Malaki 2:14-16) Limatsutsanso kusakhulupirika mu ukwati. (Ahebri 13:4) Limatero kuti ukwati nkudzipereka: ‘Chifukwa chotero mwamuna adzasiya atate wake ndi amake nadzadziphatika kwa mkazi wake: ndipo adzakhala thupi limodzi.’a—Genesis 2:24; Mateyu 19:5, 6.
-
-
Buku Lothandiza pa Moyo WamakonoBuku la Anthu Onse
-
-
a Liwu lachihebri lakuti da·vaqʹ, lotembenuzidwa kuti “nadzadziphatika” panopo, “lili ndi tanthauzo la kummamatira wina wake mwachikondi ndi mokhulupirika.”4 M’Chigiriki, liwu lotembenuzidwa kuti “nadzaphatikizana” pa Mateyu 19:5 lili paubale ndi liwu lotanthauza “kumamatiza,” “kuphatika ndi sementi,” “kulumikizana zolimba.”5
-