-
Yehova Ndi “Woulula Zinsinsi”Nsanja ya Olonda—2012 | June 15
-
-
4. Kodi mbewu ya mkazi ndi ndani, nanga mbewu imeneyi idzachita chiyani?
4 Anthu oyambirira atangopanduka m’munda wa Edeni, Yehova analonjeza kuti “mkazi” adzatulutsa “mbewu.”a (Werengani Genesis 3:15.) Analonjezanso kuti mbewu imeneyi idzaphwanya mutu wa njoka, kapena kuti Satana. Yehova anadzaulula kuti mbewuyi idzachokera mu mzera wa Abulahamu, mu mtundu wa Aisiraeli, m’fuko la Yuda ndiponso kuti idzakhala mbadwa ya Mfumu Davide. (Gen. 22:15-18; 49:10; Sal. 89:3, 4; Luka 1:30-33) Mbali yaikulu ya mbewuyi inadzakhala Khristu Yesu. (Agal. 3:16) Mbali yachiwiri ya mbewuyi ndiyo anthu odzozedwa ndi mzimu mu mpingo wachikhristu. (Agal. 3:26-29) Yesu limodzi ndi odzozedwa amapanga Ufumu wa Mulungu. Mulungu adzagwiritsa ntchito Ufumuwu kuti aphwanye Satana.—Luka 12:32; Aroma 16:20.
5, 6. (a) Kodi Danieli ndi Yohane analemba za maulamuliro amphamvu angati? (b) Kodi mitu ya chilombo chotchulidwa m’buku la Chivumbulutso imaimira chiyani?
5 Ulosi woyambirira umene Mulungu ananena mu Edeni uja unanenanso kuti Satana adzatulutsa “mbewu.” Unanena kuti mbewu yake idzadana ndi mbewu ya mkazi. Kodi mbewu ya njokayo ndi ndani? Ndi onse amene amatsanzira Satana podana ndi Mulungu ndiponso kudana ndi anthu a Mulungu. Kuyambira kalekale, Satana anakonza zoti mbewu yake izikhala ndi maufumu kapena maboma. (Luka 4:5, 6) Koma ndi maufumu ochepa okha padziko lapansi amene alowerera kwambiri m’zochita za anthu a Mulungu omwe ndi Aisiraeli ndiponso Akhristu odzozedwa. Kudziwa zimenezi kungatithandize kumvetsa chifukwa chake masomphenya a Danieli ndiponso Yohane amangonena za maulamuliro amphamvu 8 okha.
-
-
Yehova Ndi “Woulula Zinsinsi”Nsanja ya Olonda—2012 | June 15
-
-
7. Kodi mutu woyamba ukuimira ndani ndipo n’chifukwa chiyani tikutero?
7 Mutu woyamba wa chilombochi ukuimira Iguputo. Tikutero chifukwa chakuti Iguputo unali ufumu wamphamvu woyamba kudana ndi anthu a Mulungu, kapena kuti Aisiraeli. Mbewu ya mkazi yolonjezedwa inayenera kuchokera m’mbadwa za Abulahamu ndipo mbadwa zimenezi zinayamba kuchuluka kwambiri ku Iguputo. Ndiyeno ufumu wa Iguputo unayamba kupondereza Aisiraeliwo. Satana anayesa kuwononga anthu onse a Mulunguwo mbewuyo isanafike. Kodi anachita bwanji zimenezi? Iye anachititsa Farao kuganiza zoti awononge ana aamuna onse a Aisiraeli. Yehova analepheretsa zimenezi ndipo anamasula anthu ake ku ukapolo ku Iguputo. (Eks. 1:15-20; 14:13) Kenako anathandiza Aisiraeliwo kukhazikika m’Dziko Lolonjezedwa.
8. Kodi mutu wachiwiri ukuimira ndani ndipo unayesa kuchita chiyani?
8 Mutu wachiwiri wa chilombo ukuimira Asuri. Ufumu wamphamvu umenewu unayesanso kuwononga anthu onse a Mulungu. N’zoona kuti Yehova anagwiritsa ntchito Asuri polanga ufumu wa mafuko 10 a Isiraeli. Anachita zimenezi chifukwa iwo anali kulambira mafano komanso anapanduka. Koma kenako Asuri anaukiranso Yerusalemu. N’kutheka kuti Satana ankafuna kuwononga mzere wa mafumu umene Yesu anali kudzabadwira. Izi zinali zosemphana ndi cholinga cha Yehova. Choncho iye anapulumutsa anthu ake okhulupirika m’njira yozizwitsa powononga Asuriwo.—2 Maf. 19:32-35; Yes. 10:5, 6, 12-15.
-
-
Yehova Ndi “Woulula Zinsinsi”Nsanja ya Olonda—2012 | June 15
-
-
13 Yehova anagwiritsa ntchito ufumu wa Mediya ndi Perisiya pofuna kukwaniritsa ulosi. Ufumuwu unagonjetsa Babulo n’kulola Aisiraeli kubwerera kwawo. (2 Mbiri 36:22, 23) Koma pa nthawi ina, ufumu womwewu unangotsala pang’ono kuwononga anthu onse a Mulungu. M’buku la Esitere muli nkhani ya chiwembu chimene nduna yaikulu ya ufumu wa Perisiya, dzina lake Hamani, anakonza. Iye anakonza zoti Ayuda onse amene anali m’zigawo zolamulidwa ndi ufumu wa Perisiya aphedwe. Ndipo iye anakonzeratu tsiku loti chiwembuchi chichitike. Koma Yehova analowererapo n’kupulumutsa anthu ake kuti asawonongedwe ndi mbewu ya Satana. (Esitere 1:1-3; 3:8, 9; 8:3, 9-14) Choncho, m’pomveka kunena kuti ufumu wa Mediya ndi Perisiya ukuimiridwa ndi mutu wachinayi wa chilombo cha m’buku la Chivumbulutso.
-
-
Yehova Ndi “Woulula Zinsinsi”Nsanja ya Olonda—2012 | June 15
-
-
16. Kodi Antiyokasi Wachinayi anachita zotani?
16 Ufumu wa Girisi utagonjetsa Perisiya, unayamba kulamulira dziko limene anthu a Mulungu ankakhala. Pa nthawiyi, Ayuda anali atabwerera ku Dziko Lolonjezedwa ndipo anali atamanganso kachisi ku Yerusalemu. Ayudawo anali adakalibe anthu osankhidwa a Mulungu ndipo kachisi amene anamumanganso uja ndi amene anali malo awo olambirira. Koma m’zaka za m’ma 100 B.C.E., ufumu wa Girisi, womwe ndi mutu wachisanu wa chilombo chija, unaukira anthu a Mulungu. Antiyokasi Wachinayi anali mmodzi wa asilikali amene analowa m’malo mwa Alekizanda. Iye anaika guwa lansembe loperekera nsembe kwa milungu yonyenga m’bwalo la kachisi ku Yerusalemu. Analamula kuti munthu aliyense wotsatira chipembedzo chachiyuda aphedwe. Izi zikusonyeza kuti mbewu ya Satana inali kudana kwambiri ndi anthu a Mulungu. Koma posapita nthawi, ufumu wa Girisi unalowedwa m’malo ndi ulamuliro wina wamphamvu padziko lonse. Kodi mutu wa 6 ukuimira ufumu uti?
-
-
Yehova Ndi “Woulula Zinsinsi”Nsanja ya Olonda—2012 | June 15
-
-
17. Kodi mutu wa 6 unachita chiyani chokhudza kukwaniritsidwa kwa ulosi wa pa Genesis 3:15?
17 Pa nthawi imene Yohane ankaona masomphenya a chilombo, ufumu wa Roma ndi umene unali wamphamvu. (Chiv. 17:10) Mutu wa 6 umenewu unachita chinthu chachikulu chokhudza kukwaniritsidwa kwa ulosi wa pa Genesis 3:15. Satana anagwiritsa ntchito asilikali achiroma kuti avulaze “chidendene” cha mbewu yolonjezedwa. Kodi anachita bwanji zimenezi? Iwo anaimba Yesu mlandu wabodza woukira boma ndipo anamupha. (Mat. 27:26) Koma bala limeneli linachira mwamsanga chifukwa Yehova anaukitsa Yesu.
18. (a) Kodi Yehova anasankha mtundu watsopano uti ndipo n’chifukwa chiyani? (b) Kodi mbewu ya njoka inasonyeza bwanji kuti inkalusirabe mbewu ya mkazi?
18 Atsogoleri achipembedzo a Isiraeli anagwirizana ndi Aroma pokonzera Yesu chiwembu ndipo Ayuda ambiri anakana Yesu. Choncho, Yehova anasiya kuona mtundu wa Isiraeli ngati anthu ake. (Mat. 23:38; Mac. 2:22, 23) M’malomwake, anasankha mtundu watsopano womwe ndi “Isiraeli wa Mulungu.” (Agal. 3:26-29; 6:16) Mtundu watsopanowu ndi wa Akhristu odzozedwa ndipo wapangidwa ndi Ayuda komanso anthu amitundu ina. (Aef. 2:11-18) Yesu atafa n’kuukitsidwa, mbewu ya njoka inapitirizabe kulusira mbewu ya mkazi. Aroma anayesanso kuwononga mpingo wa Akhristu odzozedwa, womwe ndi mbali yachiwiri ya mbewu ya mkazi.c
-
-
Yehova Ndi “Woulula Zinsinsi”Nsanja ya Olonda—2012 | June 15
-
-
a Mkazi ameneyu amaimira gulu la Yehova la zolengedwa zauzimu zakumwamba lomwe lili ngati mkazi wake.—Yes. 54:1; Agal. 4:26; Chiv. 12:1, 2.
-
-
Yehova Ndi “Woulula Zinsinsi”Nsanja ya Olonda—2012 | June 15
-
-
c Ngakhale kuti Aroma anawononga Yerusalemu mu 70 C.E., izi sizinakwaniritse ulosi wa pa Genesis 3:15. Pa nthawiyi, mtundu wa Isiraeli sunali anthu osankhidwa a Mulungu.
-