-
Kodi Moyo Unayamba Bwanji?Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
-
-
3. Kodi n’chiyani chimasiyanitsa anthu ndi nyama?
Yehova atalenga dzikoli, analenganso zinthu zamoyo. Choyamba analenga zomera ndi nyama. Kenako “Mulungu analenga munthu m’chifaniziro chake.” (Werengani Genesis 1:27.) Kodi n’chiyani chimachititsa kuti anthu azisiyana ndi nyama? Anthufe timatha kukhala ndi makhalidwe abwino monga chikondi ndi chilungamo chifukwa chakuti tinalengedwa m’chifaniziro cha Mulungu. Iye anatilenganso ndi luso lotha kuphunzira zinenero, kusangalala ndi nyimbo komanso zinthu zina zokongola. Ndipo mosiyana ndi zinyama, anthufe timatha kulambira Mlengi wathu.
-
-
Kodi Moyo Unayamba Bwanji?Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
-
-
5. Nkhani ya m’Baibulo yokhudza kulengedwa kwa zinthu ndi yoona
Mu Genesis chaputala 1, Baibulo limafotokoza mmene dziko lapansi komanso zinthu zamoyo zinayambira. Kodi inuyo mumakhulupirira nkhani imeneyi, kapena mumaona kuti ndi yongopeka? Onerani VIDIYO, kenako mukambirane mafunso otsatirawa:
Kodi Baibulo limaphunzitsa kuti dziko lapansi ndiponso zamoyo zonse zinalengedwa m’masiku 6 a maola 24?
Kodi inuyo mumaona kuti nkhani ya m’Baibulo yokhudza kulengedwa kwa zinthu ndi yomveka komanso yoona? N’chifukwa chiyani mukutero?
Werengani Genesis 1:1, kenako mukambirane funso ili:
Asayansi amanena kuti chilengedwechi chili ndi chiyambi. Kodi zimene amanenazi zikugwirizana bwanji ndi zimene mwawerenga m’Baibulo?
Anthu ena amaganiza kuti polenga zinthu, Mulungu anangochititsa kuti zisinthe kuchokera ku zinthu zina. Werengani Genesis 1:21, 25, 27, kenako mukambirane mafunso awa:
Kodi Baibulo limaphunzitsa kuti Mulungu anapanga zinthu zing’onozing’ono zomwe zinasintha n’kukhala nsomba, zinyama ndiponso anthu? Kapena kodi analenga zamoyo za “mitundu” yosiyanasiyana?b
-