-
“Nthaŵi Yolankhula”—Liti?Nsanja ya Olonda—1987
-
-
Chitsogozo china cha Baibulo chimapezeka pa Levitiko 5:1: “Ndipo akachimwa munthu, wakuti adamva mawu akuwalumbiritsa, ndiye mboni, kapena wakuwona, kapena wakudziŵa, koma osaulula, azisenza mphulupulu yake.” “Kumva mawu akulumbiritsa” kumeneku sikunali koipa kapena konyansa. M’malo mwake, kaŵirikaŵiri chinali kuti pamene winawake analakwiridwa anakakamiza kuti mboni yoyenerera imthandiza iye kupeza chilungamo, pamene anali kulumbiritsa—mwachidziŵikire kuchokera kwa Yehova—pa wina wake, mwinamwake mosazindikiritsidwa, amene adamulakwira iye. Unali mtundu wakuika ena pansi pa chilumbiro. Wochitira umboni aliyense wa cholakwacho akadziŵa amene anavutika ndi kupanda chilungamo ndipo akakhala ndi thayo la kubwera kudzakhazikitsa cholakwacho. Kupanda apo, iwo anayenera ‘kuyankha kaamba ka zolakwa zawo’ pamaso pa Yehova.b
Chiweruzo chimenechi chochokera ku Malo Apamwamba koposa aulamuliro mu chilengedwe amaika thayo pa aliyense wa Aisrayeli kupereka ripoti kwa oweruza cholakwa chirichonse chowopsya chomwe anawona kotero kuti nkhaniyo isamaliridwe. Pamene kuli kwakuti Akristu sali mokakamizika pansi pa Chilamulo cha Mose, maprinsipulo ake amagwirabe ntchito ku mpingo Wachikristu. Chotero, pangakhale nthaŵi pamene Mkristu amakhala ndi thayo lakubweretsa nkhani ku chisamaliro cha akulu. Zowona, chiri cholakwa m’maiko ambiri kudziŵitsa anthu osayeneretsedwa zinthu zomwe zikupezedwa mu zolembera za mseri. Koma ngati Mkristu adzimva, pambuyo pa kulingalira kwa pemphero, kuti iye akuyang’anizana ndi mkhalidwe umene lamulo la Mulungu likumufuna iye kupereka ripoti la chimene iye akudziŵa mosasamala kanthu za malamulo a olamulira ocheperako, pamenepo liri thayo limene alandira kwa Yehova. Pamakhala nthaŵi pamene Akristu “ayenera kumvera Mulungu osati anthu.”—Machitidwe 5:29.
Pamene kuli kwakuti zilumbiro kapena malonjezo enieni sayenera kutengedwa mopepuka, pangakhale pamene malonjezo ofunikira kwa anthu ali owombana ndi chifuno chakupereka kudzipereka kotheratu kwa Mulungu wathu. Pamene winawake achita chimo lalikulu, iye, m’chenicheni, amafika pansi pa ‘kulumbiritsidwa kwapoyera’ kuchokera kwa mmodzi wa wolakwiridwayo, Yehova Mulungu. (Deuteronomo 27:26; Miyambo 3:33) Onse amene amakhala mbali ya mpingo Wachikristu amadziika iwo eni pansi pa “lumbiro” kusunga mpingo kukhala woyera, ponse paŵiri mwa zimene iwo amachita mwaumwini ndi njira imene iwo amathandizira ena kukhalabe oyera.
-
-
“Nthaŵi Yolankhula”—Liti?Nsanja ya Olonda—1987
-
-
b Mu Commentary on the Old Testament, Keil ndi Delitzsch ananena kuti munthu angakhale wolakwa kapena kuchimwa ngati “anadziŵa upandu wa wina, kaya anawona iwo, kapena anafika kuchidziŵitso chinachake cha icho mwanjira ina yake, ndipo kuti chotero anali woyeneretsedwa kuwonekera pabwalo la mlandu monga mboni kaamba ka kutsimikizira upanduwo, ananyalanyaza kuchita tero, ndipo sananene chimene iye anawona kapena kudziŵa, pamene iye anamva chiweruzo chotheratu cha woweruza pa kufufuza kwapoyera kwa upanduwo, pa chimene anthu onse amene alipo, omwe anadziŵa chirichonse cha nkhaniyo, anafulumizidwa kubwera monga mboni.”
-