Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w05 3/15 tsamba 30
  • Mafunso Ochokera kwa Owerenga

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Mafunso Ochokera kwa Owerenga
  • Nsanja ya Olonda—2005
  • Nkhani Yofanana
  • Kubudula Ngala pa Sabata
    Nsanja ya Olonda—1987
  • Kubudula Ngala pa Sabata
    Munthu Wamkulu Woposa Onse Amene Anakhalako
  • Anabudula Ngala za Tirigu pa Tsiku la Sabata
    Yesu—Ndi Njira, Choonadi ndi Moyo
  • Mafunso Ochokera kwa Oŵerenga
    Nsanja ya Olonda—1994
Nsanja ya Olonda—2005
w05 3/15 tsamba 30

Mafunso Ochokera kwa Owerenga

Kodi kudya mkate wopatulika kwa Davide ndi anyamata ake kumasonyeza kuti ngati zinthu zavuta munthu angaswe lamulo la Mulungu koma osalangidwa?​—1 Samueli 21:1-6.

Malinga ndi lemba la Levitiko 24:5-9, mkate wopatulika womwe anali kuuchotsa tsiku la Sabata lililonse ndi kuikapo watsopano, unayenera kudyedwa ndi ansembe okha basi. Ansembe okha ndi amene anali oyenera kudya mkatewo chifukwa chakuti unali wopatulika ndipo umayenera kukhala chakudya cha anthu omwe akutumikira Mulungu. Kuupereka kwa munthu wamba kapena kudya mwachisawawa kunali kulakwa. Komabe, wansembe Ahimeleki sanalakwe pamene anagawira Davide ndi anyamata ake mkate wopatulikawo.

Ahimeleki anaona kuti Davide anali kugwira ntchito yapadera motumidwa ndi Mfumu Sauli. Davide ndi anyamata akewo anamva njala. Ahimeleki anatsimikizira kuti iwo anali oyera. Ngakhale kuti anachita zosemphana ndi chilamulo mwa kudya mkate wopatulikawo, zinali zogwirizana ndi cholinga cha mkate wopatulikawo. Ahimeleki anaganizira zimenezi posankha kusatsatira lamulo limeneli. Ngakhalenso Yesu Kristu anatchula nkhani imeneyi monga chitsanzo chosonyeza kuti sikunali koyenera kukhwimitsa chilamulo cha Sabata monyanyira monga mmene Afarisi ankachitira.​—Mateyu 12:1-8.

Komatu zimenezi sizikutanthauza kuti ngati zinthu zavuta, n’zololeka kuswa lamulo la Mulungu ayi. Mwachitsanzo, pamene asilikali a Israyeli anali kumenyana ndi Afilisti, zikuoneka kuti zinthu zinafika povuta. Mfumu Sauli inali itanena kuti: “Atembereredwe iye wakudya kanthu kufikira madzulo, ndikabwezere chilango adani anga.” Baibulo limanena kuti: “Anakantha Afilisti tsiku lija.” Asilikaliwo anatopa chifukwa cha kumenyanako ndipo anamva njala, mwakuti ‘anthuwo anatenga nyama, naziphera pansi; nazidya zili ndi mwazi wawo.’ (1 Samueli 14:24, 31-33) Anthuwo anachimwira Yehova mwa kuswa lamulo lake pankhani ya magazi. Zomwe anachitazo zinali zosemphana ndi njira yokha yogwiritsira ntchito magazi imene Mulungu analamula yomwe ndi ‘kutetezera’ machimo. (Levitiko 17:10-12; Genesis 9:3, 4) Mwa chifundo chake, Yehova, analandira nsembe zapadera zomwe zinaperekedwa chifukwa cha ochimwawo.​—1 Samueli 14:34, 35.

Inde, Yehova amafuna kuti tizimvera malamulo ake kaya zinthu zili bwino kapena ayi. Mtumwi Yohane anati: “Ichi ndi chikondi cha Mulungu, kuti tisunge malamulo ake.”​—1 Yohane 5:3.

[Chithunzi patsamba 30]

Sabata lililonse, ankaika mikate yopatulika yatsopano mu chihema

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena