Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Anapemphera Kuchokera Pansi pa Mtima
    Tsanzirani Chikhulupiriro Chawo
    • 9. Kodi tikuphunzira chiyani pa zimene Hana anachita popitabe ku Silo ngakhale kuti ankadziwa zoti mkazi mnzake azikamunyoza?

      9 M’mawa wa tsiku la ulendoli, banja lonse la Elikana, linali pakalikiliki kukonzekera. Banja lalikululi linkakonzekera ulendo wa makilomita oposa 30 wopita ku Silo, kudutsa m’mapiri a ku Efraimu.b Kwa munthu woyenda pansi, ulendowu unali wa tsiku limodzi kapena masiku awiri. Hana ankadziwa kuti mkazi mnzake azikamunyoza, koma anapitabe. Pamenepatu iye anasonyeza chitsanzo chabwino kwambiri kwa anthu olambira Mulungu masiku ano. Si bwino kulola khalidwe loipa la anthu ena kutilepheretsa kulambira Mulungu. Ngati titachita zimenezi zingatilepheretse kulandira madalitso amene angatithandize kupirira mavuto.

  • Anapemphera Kuchokera Pansi pa Mtima
    Tsanzirani Chikhulupiriro Chawo
    • b Mtunda umenewu tikutengera kuti mwina kwawo kwa Elikana kunali ku Rama, komwe m’nthawi ya Yesu kunkadziwika ndi dzina lakuti Arimateya.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena