-
Anali Watcheru Ndiponso AnadikiraNsanja ya Olonda—2008 | April 1
-
-
Eliya anapita kwa Ahabu n’kumuuza kuti: “Nyamukani, idyani, imwani; popeza kumveka mkokomo wa mvula yambiri.” (Vesi 41) Kodi mfumu yoipayi inali itaphunzirapo kanthu pa zimene zinachitika patsikuli? Nkhaniyi siinena mwachindunji, koma timaona umboni wakuti iye sanalape ndiponso sanapemphe mneneriyu kuti am’pempherere kwa Yehova n’cholinga choti am’khululukire. M’malomwake, “Ahabu anapita kukadya, ndi kumwa.” (Vesi 42) Nanga Eliya anatani?
-
-
Anali Watcheru Ndiponso AnadikiraNsanja ya Olonda—2008 | April 1
-
-
Eliya anali ndi chidwi chofuna kudziwa umboni wosonyeza kuti Yehova anali atatsala pang’ono kuthetsa chilala. Motero anatuma mnyamata wake kuti akwere pamwamba penipeni pa phirilo n’cholinga choti aone kutali ngati kunali zizindikiro zoti mvula ingagwe. Mnyamatayo atabwerako, anauza Eliya uthenga wosalimbikitsa woti: “Kulibe kanthu.” Kunja kunali kuli mbee, kopanda mitambo. Koma kodi mwaona chinachake chapadera pankhani imeneyi? Kumbukirani kuti Eliya anali atangouza kumene mfumu Ahabu kuti: ‘Kukumveka mkokomo wa mvula yambiri.’ Kodi n’chiyani chinachititsa mneneriyu kunena zimenezi pomwe kunja kunali kopanda mitambo?
Eliya ankadziwa bwino zimene Yehova anali atalonjeza. Popeza iye anali mneneri ndiponso woimira Mulungu, ankakhulupirira kuti Mulungu akwaniritsa zimene analonjeza. Eliya anali ndi chikhulupiriro cholimba kwambiri moti ankangokhala ngati akumva mkokomo wamvula. Zimenezi zikutikumbutsa nkhani ya m’Baibulo yokhudza Mose. Nkhaniyo imati: “Anapitirizabe kukhala wochirimika ngati kuti akuona Wosaonekayo.” Kodi inuyo mumaona kuti Mulungu ndi weniweni? Iye watipatsa zifukwa zomveka bwino zoti tim’khulupirire iye ndiponso malonjezo ake.—Aheberi 11:1, 27.
-