-
Chitsanzo cha Kudzimana ndi KukhulupirikaNsanja ya Olonda—1997 | November 1
-
-
KWA mlimi wina wachinyamata wotchedwa Elisa, tsiku lolima limene linayamba monga mwa nthaŵi zonse linasintha kukhala tsiku lapadera kwambiri m’moyo wake. Pamene anali kulima m’munda, Elisa anachezeredwa mwadzidzidzi ndi Eliya, mneneri wamkulu wa Israyeli. ‘Kodi angafunenji kwa ine?’ Mwina Elisa anadzifunsa motero. Sipanapite nthaŵi yaitali asanapeze yankho. Eliya anaponya chofunda chake kwa Elisa, kusonyeza kuti tsiku lina Elisa adzaloŵa paulendo wakewo. Elisa sanatenge chiitanochi mopepuka. Nthaŵi yomweyo, anasiya munda wake nakhala mnyamata wa Eliya.—1 Mafumu 19:19-21.
-
-
Chitsanzo cha Kudzimana ndi KukhulupirikaNsanja ya Olonda—1997 | November 1
-
-
Ataitanidwa ndi Eliya ku utumiki wapadera, Elisa nthaŵi yomweyo anasiya munda wake napita kukatumikira mneneri wamkulu wa Israyeli. Mwachionekere, ntchito zake zina zinali zapansi, popeza anadzadziŵika monga amene “anathira madzi m’manja a Eliya.”c (2 Mafumu 3:11) Komabe, Elisa anaona ntchito yake kukhala mwaŵi, ndipo mokhulupirika anamamatira ku mbali ya Eliya.
Atumiki ambiri a Mulungu lerolino amasonyeza mzimu wofananawo wodzimana. Ena asiya “minda” yawo, njira zawo zopezera ndalama, kuti akalalikire uthenga wabwino kumagawo akutali kapena kukatumikira monga mamembala a banja la Beteli. Ena apita ku maiko achilendo kukagwira ntchito kumene Sosaite ikumanga. Ambiri alandira zimene zingatchedwe ntchito zapansi. Komabe, palibe kapolo wa Yehova amene akuchita utumiki waung’ono. Yehova amayamikira onse amene amamtumikira mofunitsitsa, ndipo adzadalitsa mzimu wawo wodzimana.—Marko 10:29, 30.
-