Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w15 4/15 tsamba 32
  • Mtengo Ukadulidwa Umaphukanso?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Mtengo Ukadulidwa Umaphukanso?
  • Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
  • Nkhani Yofanana
  • Yobu Sankakayikira Kuti Akufa Adzauka
    Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2016
  • Mtengo Wauŵisi wa Azitona M’nyumba ya Mulungu
    Nsanja ya Olonda—2000
  • ‘Nzeru za Mulungu N’zozama’ Kwambiri
    Nsanja ya Olonda—2011
  • Mafuta a Golide a ku Mediterranean
    Galamukani!—2008
Onani Zambiri
Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova—2015
w15 4/15 tsamba 32
Mtengo ukadulidwa umaphukanso

Mtengo Ukadulidwa Umaphukanso

MTENGO wa maolivi suoneka bwino tikauyerekezera ndi wa mkungudza. Koma mtengo wa maolivi umapirira nyengo zovuta kwambiri. Ena apezapo mitengo yotereyi yomwe yakhala zaka 1,000. Mtengowu umakhala ndi mizu italiitali ndipo izi zimachititsa kuti ukadulidwa uphukenso.

Yobu ankakhulupirira kuti akafa adzaukanso. (Yobu 14:13-15) Posonyeza kuti amakhulupirira zoti Mulungu adzaukitsa anthu iye ananena kuti: “Ngakhale mtengo umakhala ndi chiyembekezo. Ukadulidwa umaphukanso.” N’kutheka kuti Yobu analemba zimenezi akuganizira za mtengo wa maolivi. Kukachitika chilala, mtengowu ukhoza kuuma koma mizu yake siifa. Ndipo mvula ikabwera nthambi zimaphuka “ngati mtengo watsopano.”—Yobu 14:7-9.

Mlimi amalakalaka kuona mtengo wa maolivi umene unadulidwa ukuphuka. Nayenso Yehova amalakalaka kuukitsa anthu amene amwalira. (Mat. 22:31, 32; Yoh. 5:28, 29; Mac. 24:15) Tidzasangalala kwambiri kuona anzathu atauka.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena