Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Ukulu wa Yehova ndi Wosasanthulika
    Nsanja ya Olonda—2004 | January 15
    • Makhalidwe a Mulungu Ndi Aakulu Koposa!

      20, 21. (a) Lemba la Salmo 145:7-9 limasonyeza bwino kwambiri ukulu wa Yehova mwa kunena za makhalidwe ati? (b) Kodi makhalidwe a Mulungu otchulidwa pamenepa amawakhudza bwanji onse amene amam’konda?

      20 Monga mmene taonera, mavesi oyambirira asanu ndi limodzi a Salmo 145 amatipatsa zifukwa zomveka zolemekezera Yehova chifukwa cha zinthu zokhudza ukulu wake wosasanthulika. Mavesi 7 mpaka 9 amasonyeza bwino kwambiri ukulu wa Mulungu mwa kunena za makhalidwe ake. Davide anaimba kuti: “Adzabukitsa chikumbukiro cha ubwino wanu waukulu, nadzaimbira chilungamo chanu. Yehova ndiye wachisomo, ndi wachifundo; wosakwiya msanga, ndi wa chifundo chachikulu [“wokoma mtima mwachikondi kwambiri,” NW]. Yehova achitira chokoma onse; ndi nsoni zokoma zake zigwera ntchito zake zonse.”

      21 Pamenepa Davide choyamba anafotokoza ubwino ndi chilungamo cha Yehova, makhalidwe amene Satana Mdyerekezi anakayikira. Kodi makhalidwe ameneŵa amawakhudza bwanji onse amene amakonda Mulungu ndi kugonjera ulamuliro wake? Ndithudi, ubwino wa Yehova ndi kulamulira kwake kolungama zimasangalatsa olambira ake moti sangasiye kum’lemekeza. Ndipo ubwino wa Yehova umapita kwa “onse.” Tikukhulupirira kuti zimenezi zidzathandiza anthu ambiri kulapa ndi kukhala olambira Mulungu woona madzi asanafike m’khosi.​—Machitidwe 14:15-17.

      22. Kodi Yehova amachita bwanji ndi atumiki ake?

      22 Davide anayamikiranso kwambiri makhalidwe amene Mulungu anatchula pamene “anapita pamaso pa [Mose], nafuula, Yehova, Yehova, Mulungu wachifundo ndi wachisomo, wolekereza, ndi wa ukoma mtima wochuluka, ndi wachoonadi.” (Eksodo 34:6) Motero, Davide anati: ‘Yehova ndiye wachisomo, ndi wachifundo; wosakwiya msanga, ndi wokoma mtima mwachikondi kwambiri.’ Ngakhale kuti ukulu wa Yehova ndi wosasanthulika, amalemekeza anthu omutumikira mwa kuwasonyeza chisomo. Iye ndi wachifundo kwambiri ndipo ali wofunitsitsa kukhululukira ochimwa olapa pamaziko a nsembe ya dipo ya Yesu. Yehova alinso wosakwiya msanga chifukwa amapatsa atumiki ake mpata wothetsa zofooka zimene zingawalepheretse kuloŵa m’dziko lake lolungama.​—2 Petro 3:9, 13, 14.

  • Chikondi Chokhulupirika cha Yehova N’chachikulu
    Nsanja ya Olonda—2004 | January 15
    • Chikondi Chokhulupirika cha Yehova N’chachikulu

      “Yehova . . . ndi wa chifundo chachikulu [“wokoma mtima mwachikondi kwambiri,” NW].”​—SALMO 145:8.

      1. Kodi chikondi cha Mulungu n’chachikulu bwanji?

      “MULUNGU ndiye chikondi.” (1 Yohane 4:8) Mawu osangalatsa ameneŵa amatsimikizira kuti Yehova amalamulira mwachikondi. Inde, ngakhale anthu amene samumvera amapindula ndi dzuŵa ndiponso mvula zimene amapereka mwachikondi. (Mateyu 5:44, 45) Chifukwa choti Mulungu amakonda anthu, ngakhale adani ake angalape n’kubwerera kwa iye ndi kupeza moyo wosatha. (Yohane 3:16) Koma posachedwapa, Yehova adzawononga oipa omwe sangasinthe kuti anthu amene amam’konda asangalale ndi moyo wosatha m’dziko latsopano lolungama.​—Salmo 37:9-11, 29; 2 Petro 3:13.

      2. Kodi ndi mbali iti yapadera ya chikondi imene Yehova amasonyeza kwa odzipatulira kwa iye?

      2 Yehova amasonyeza chikondi kwa olambira ake mwa njira yamtengo wapatali ndiponso yokhalitsa. Mawu achihebri omasuliridwa kuti “kukoma mtima kwachikondi” kapena kuti “chikondi chokhulupirika” ndiwo amaimira chikondi chimenechi. Mfumu Davide ya Israyeli wakale inaona kukoma mtima kwachikondi kwa Mulungu kukhala kofunika kwambiri. Chifukwa cha zimene anakumana nazo ndiponso kusinkhasinkha mmene Mulungu anachitira zinthu ndi anthu ena, Davide anaimba motsimikiza kuti: ‘Yehova . . . ndi wokoma mtima mwachikondi kwambiri.’​—Salmo 145:8.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena