-
“Mphatso za Amuna” Zoperekedwa Kuti Zisamalire Nkhosa za YehovaNsanja ya Olonda—1999 | June 1
-
-
10. Kodi kukonza ena kumaphatikizapo chiyani?
10 Popereka “mphatso za amuna” kuti azitikonza, cholinga cha Yehova chinali choti akulu akhale otsitsimutsa mwauzimu ndi oyenera kutsanziridwa ndi anthu ake. (1 Akorinto 16:17, 18; Afilipi 3:17) Kukonza ena sindiko chabe kuwongolera aja ogwidwa nako kulakwa komanso kuthandiza okhulupirika kuti ayendebe molungama.a Lerolino, pokhalapo mavuto ambiri omwe amatipsinja, ambiri amafunikira kuwalimbikitsa kuti agwiritse. Ena angafunikire kuthandizidwa mwachifundo kuti akonzenso malingaliro awo m’njira ya Mulungu. Mwachitsanzo, Akristu okhulupirika ena akulimbana ndi maganizo amphamvu odziona kukhala opereŵera kapena osafunika kwenikweni. “Amantha mtima” oterowo angaganize kuti Yehova sadzawakonda konse ndi kuti ngakhale atayesetsa mwakhama chotani kutumikira Mulungu, iye sangazilandire ntchito zawo. (1 Atesalonika 5:14) Koma kalingaliridwe koteroko sikakugwirizana ndi mmene Mulungu amaoneradi alambiri ake.
-