Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • “Mphatso za Amuna” Zoperekedwa Kuti Zisamalire Nkhosa za Yehova
    Nsanja ya Olonda—1999 | June 1
    • 10. Kodi kukonza ena kumaphatikizapo chiyani?

      10 Popereka “mphatso za amuna” kuti azitikonza, cholinga cha Yehova chinali choti akulu akhale otsitsimutsa mwauzimu ndi oyenera kutsanziridwa ndi anthu ake. (1 Akorinto 16:17, 18; Afilipi 3:17) Kukonza ena sindiko chabe kuwongolera aja ogwidwa nako kulakwa komanso kuthandiza okhulupirika kuti ayendebe molungama.a Lerolino, pokhalapo mavuto ambiri omwe amatipsinja, ambiri amafunikira kuwalimbikitsa kuti agwiritse. Ena angafunikire kuthandizidwa mwachifundo kuti akonzenso malingaliro awo m’njira ya Mulungu. Mwachitsanzo, Akristu okhulupirika ena akulimbana ndi maganizo amphamvu odziona kukhala opereŵera kapena osafunika kwenikweni. “Amantha mtima” oterowo angaganize kuti Yehova sadzawakonda konse ndi kuti ngakhale atayesetsa mwakhama chotani kutumikira Mulungu, iye sangazilandire ntchito zawo. (1 Atesalonika 5:14) Koma kalingaliridwe koteroko sikakugwirizana ndi mmene Mulungu amaoneradi alambiri ake.

  • “Mphatso za Amuna” Zoperekedwa Kuti Zisamalire Nkhosa za Yehova
    Nsanja ya Olonda—1999 | June 1
    • a M’Baibulo lachigiriki lotchedwa Septuagint, verebu imodzimodzi imeneyo yomasuliridwa kuti “kukonza” inagwiritsidwa ntchito pa Salmo 17[16]:5, pamene Davide wokhulupirikayo anapemphera kuti mapazi ake ayendebe m’mabande a Yehova.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena