-
Chilengedwe Chimalengeza Ulemerero wa MulunguNsanja ya Olonda—2004 | June 1
-
-
7 Komabe, kuti munthu amve umboni umenewu pamafunika kuzindikira. “Palibe chilankhulidwe, palibe mawu; liwu lawo silimveka.” Komabe, umboni wosatulutsa mawu wa zinthu zakumwamba ndi wamphamvu kwambiri. “Muyeso wawo wapitirira pa dziko lonse lapansi, ndipo mawu awo kumalekezero a m’dziko muli anthu.” (Salmo 19:3, 4) Zili ngati kuti zakumwamba zimatumiza ‘miyeso’ pofuna kuonetsetsa kuti umboni wawo wosachita kutulutsira mawu wamveka padziko lonse lapansi.
8, 9. Kodi ndi zinthu zina ziti zodabwitsa zokhudza dzuŵa?
8 Kenako, Davide anafotokoza chinthu china chodabwitsa m’chilengedwe cha Yehova. Anati: “Iye anaika hema la dzuŵa mmenemo [m’mwamba], ndipo lili ngati mkwati wakutuluka m’chipinda mwake, likondwera ngati chimphona kuthamanga m’njira. Kutuluka kwake lituluka kolekezera thambo, ndipo kuzungulira kwake lifikira kumalekezero ake: ndipo kulibe kanthu kobisalira kutentha kwake.”—Salmo 19:4-6.
-
-
Chilengedwe Chimalengeza Ulemerero wa MulunguNsanja ya Olonda—2004 | June 1
-
-
10. (a) Kodi dzuŵa limaloŵa ndi kutuluka motani mu “hema” mwake? (b) Kodi limathamanga bwanji monga “chimphona”?
10 Wamasalmo anagwiritsa ntchito mawu okuluŵika pofotokoza za dzuŵa pamene ananena kuti dzuŵa ndi “chimphona” chimene chimathamanga kuchokera kumalekezero ena kufika malekezero ena masana, ndipo usiku chimakagona mu “hema.” Nyenyezi yaikulu imeneyi ikamaloŵa kumadzulo, munthu akamaiona ali padziko lapansi imaoneka ngati imapita mu “hema,” ngati kuti ikukapuma. Kum’maŵa imaoneka ngati ikutumphuka, n’kuwala kwambiri “ngati mkwati wakutuluka m’chipinda mwake.” Popeza anali mbusa, Davide ankadziŵa kuti usiku kunali kuzizira kwambiri. (Genesis 31:40) Anali kukumbukira kuti dzuŵa linkamuchititsa kumva kutenthera mofulumira komanso kutenthetsa malo amene iye anali. Mwachionekere, silinali kutopa pa “ulendo” wake wochoka kum’maŵa kufika kumadzulo koma linali ngati “chimphona,” chokonzeka kubwerezanso ulendo wake.
-