-
‘Kondwerani mwa Yehova’Nsanja ya Olonda—2003 | December 1
-
-
“Usachite Nsanje”
3, 4. Kodi Davide akutilangiza chiyani malinga ndi mmene Salmo 37:1 likunenera, ndipo n’chifukwa chiyani kumvera langizo limeneli n’koyenera masiku ano?
3 Tikukhala ‘m’nthaŵi zoŵaŵitsa’ ndipo pali zoipa zambiri zimene zikuchitika. Takhala tikuona zimene mtumwi Paulo ananena zikuchitikadi. Iye anati: “Anthu oipa ndi onyenga, adzaipa chiipire, kusokeretsa ndi kusokeretsedwa.” (2 Timoteo 3:1, 13) Tikhoza kukhudzidwa mosavuta ndi mmene anthu oipa akuonekera ngati zinthu zikuwayendera bwino ndiponso akutukuka. Zonsezi zingatidodometse, kutichititsa kuti kuona kwathu zinthu mwauzimu kusokonezeke. Onani mmene mawu oyamba a Salmo 37 akutichenjezera za ngozi imeneyi yomwe tikhoza kukumana nayo. Akuti: “Usavutike mtima chifukwa cha ochita zoipa, usachite nsanje chifukwa cha ochita chosalungama.”
4 Tsiku ndi tsiku, mawailesi, ma TV, ndi manyuzipepala amatiuza zinthu zambirimbiri zosonyeza kusoŵa chilungamo. Anthu amalonda osaona mtima salangidwa chifukwa cha chinyengo chawo. Zigaŵenga zimapezerera anthu osavuta kuwadyera masuku pamutu. Anthu amene amapha anzawo satulukiridwa kapena salangidwa. Zitsanzo zonsezi za kusoŵa chilungamo zingatikwiyitse ndi kusokoneza mtendere wathu wa maganizo. Popeza anthu oipa akuoneka ngati zinthu zikuwayendera bwino, zimenezi zikhoza kutichititsa kukhala ndi mtima wa nsanje. Koma kodi kuipidwa kwathu kudzathandiza kuti zinthu zisinthe? Kodi kuchitira nsanje anthu oipa omwe akuoneka ngati zinthu zikuwayendera bwino kudzasintha zinthu kuti zisawayendere bwino? Ayi! Ndipo palibedi chifukwa choti ‘tivutike mtima.’ N’chifukwa chiyani sitiyenera kutero?
-
-
‘Kondwerani mwa Yehova’Nsanja ya Olonda—2003 | December 1
-
-
6. Kodi tikuphunzira chiyani pa Salmo 37:1, 2?
6 Motero, kodi tilole kuti kutukuka kosakhalitsa kwa anthu oipa kutidodometse? Phunziro limene lili m’mavesi aŵiri oyambirira a Salmo 37 n’lakuti: Musalole kusiya njira imene munasankha yotumikira Yehova chifukwa chakuti anthu oipa zinthu zikuwayendera bwino. M’malo mwake, ikani mtima pa madalitso ndi zolinga zauzimu.—Miyambo 23:17.
-