-
Ulamuliro wa “Kalonga wa Mtendere” Pakati pa Adani AkeChisungiko cha Padziko Lonse mu Ulamuliro wa “Kalonga wa Mtendere”
-
-
4-6. (a) Kodi ndimotani mmene Salmo 2 mofananamo limasonyezera kuti Yesu sanafunikire kuyembekezera kutembenuzidwa kwa dziko asanayambe kulamulira kwake monga “Kalonga wa Mtendere”? (b) Kodi ndipanthaŵi iti pamene Salmo 2:7 linakwaniritsidwa?
4 Pamenepa, mwachiwonekere, Yesu Kristu, monga Mwana wa Davide, sanali kudzayamba kulamulira pambuyo pa kutembenuka kwadziko. Mmalo mwake, iye anali kudzayamba kulamulira pakati pa adani amene Yehova Mulungu potsirizira pake mwa nkhondo akawapangitsa kukhala chopondapo mapazi cha Mwana wake woikidwa pampando wachifumu. Mofananamo Salmo 2, m’mawu otsatira, likusonyeza chiyambi cha ulamuliro wake monga “Kalonga wa Mtendere” pakati pa adani:
5 “Aphokoseranji amitundu, nalingiliranji anthu zopanda pake? Adzikhazikitsa mafumu adziko lapansi, nachita upo akulu pamodzi, kutsutsana naye Yehova, ndi Wodzozedwa wake, [Kristu Wake], ndi kuti, Tidule zomangira zawo, titaye nsinga zawo. Wokhala m’mwambayo adzaseka; Ambuye adzawanyoza. Pomwepo adzalankhula nawo mu mkwiyo wake, nadzawawopsa mu ukali wake: Koma Ine ndadzoza mfumu yanga pa Ziyoni, phiri langa loyera.
-
-
Ulamuliro wa “Kalonga wa Mtendere” Pakati pa Adani AkeChisungiko cha Padziko Lonse mu Ulamuliro wa “Kalonga wa Mtendere”
-
-
7. Kodi ndikugwira mawu kwa Salmo 2 kotani kumene atumwi a Yesu Kristu anapanga pambuyo pa tsiku la Pentekoste?
7 Mogwirizana ndi kunena kwa Machitidwe 4:24-27, atumwi a Yesu Kristu anagwira mawu salmo lachiŵiri limeneli pambuyo pa tsiku la Pentekoste, 33 C.E. kuti: “Anakweza mawu kwa Mulungu ndi mtima umodzi, nati, Mfumu, ndinu wolenga thambo lakumwamba ndi dziko, ndi nyanja, ndi zonse ziri mmenemo; amene mwa mzimu woyera, pakamwa pa kholo lathu Davide mtumiki wanu, mudati, Amitundu asokosera chifukwa chiyani? Nalingilira zopanda pake anthu? Anadzindandalitsa mafumu a dziko, ndipo oweruza anasonkhanitsidwa pamodzi, kutsutsana ndi Ambuye ndi Kristu wake. Pakuti zowonadi anasonkhanidwa m’mudzi muno Herode, ndi Pontiyo Pilato yemwe pamodzi ndi amitundu ndi anthu a Israyeli kumchitira choipa Mwana wanu wopatulika Yesu amene munamdzoza.”
Kukawaniritsidwa Kwakukulu kwa Salmo 2
8. (a) Kodi ndiliti pamene kukwaniritsidwa koyamba kwa Salmo 2:1, 2 kunachitika? (b) Kodi nkuyambira liti pamene kukwaniritsidwa kwakukulu kwa Salmo 2 kwakhala kukuchitika?
8 Kukwaniritsidwa koyamba kwa mawu olosera amenewo a Salmo 2:1, 2 kunachitika m’chaka cha 33 cha zaka za zana loyamba. Kumeneku kunaphatikizapo munthuyo Yesu Kristu padziko lapansi. Iye anali atadzozedwa ndi mzimu woyera wa Yehova panthaŵi ya ubatizo wake ndi Yohane Mbatizi. Koma kukwaniritsidwa kwakukulu kwa Salmo 2 kwachitika chiyambire mapeto a Nthaŵi za Akunja m’chaka cha 1914. (Luka 21:24) Kwatsimikiziridwa mokwanira kuti “nthaŵi zoikidwiratu za amitundu,” zimene zinayamba pa chiwonongeko choyamba cha mzinda wa Yerusalemu mu 607 B.C.E., zinatha m’chaka cha 1914.a Pamenepo mitundu ya dziko lino, kuphatikizapo ya Dziko Lachikristu inachenjezedwa za imfa.
9. Kodi nchiyani chimene chinachitika pa chiwonongeko choyamba cha Yerusalemu ponena za Ufumu wa Mulungu monga momwe unaimiridwira ndi mzera wachifumu wa Mfumu Davide?
9 Pa chiwonongeko choyamba cha Yerusalemu, chochitidwa ndi Ababulo, Ufumu wa Yehova Mulungu pamtundu wa Israyeli, monga momwe unaimiridwira ndi mzera wachifumu wa Davide, unatha. Kuyambira pamenepo, Ayuda akuthupi sanakhale ndi mfumu ya mzera wa nyumba yachifumu ya Davide. Koma Ufumu wa Mulungu Wam’mwambamwamba m’manja mwa mbadwa ya Davide, amene Yehova anachita naye pangano la Ufumu wosatha m’mzera wake, sunali kudzakhala wosagwira ntchito kosatha padziko lapansi.
10, 11. (a) Kodi nchiyani chimene Mulungu kudzera mwa mneneri wake Ezekieli adanena ponena za mpando wachifumu wa Davide? (b) Kodi ndani amene anafika ndi “kuyenera” kwa kukhala pampando wachifumu wa Davide? (c) Kodi nchiyani chimene khamu la Ayuda lidanena pamene iye anadzipereka kukhala woloŵa nyumba walamulo?
10 Mwamsanga chiwonongeko chake choyamba chisanachitike, Yehova anachititsa mneneri wake Ezekieli kulunjikitsa mawu aŵa kwa mfumu ya Yerusalemu wakale: “Ndipo iwe wolasidwa woipa, kalonga wa Israyeli, amene lafikira tsiku lako, nthaŵi ya mphulupulu yotsiriza; atero Ambuye Yehova, Chotsa zilemba, vula korona, ufumu sudzakhalanso momwemo, kweza chopepuka, tchepsa chokwezeka. Ndidzagubuduza gubuduza gubuduza ufumu uno, sudzakhalanso kufikira akadza iye mwini chiweruzo; ndipo ndidzaupereka kwa iye.”—Ezekieli 21:25-27.
11 Iye amene ali “mwini chiweruzo” anadza monga munthu Yesu Kristu, ndipo mzera wake wobadwiramo wa Davide walembedwa pa Mateyu 1:1-16 ndi pa Luka 3:23-31. Kaŵirikaŵiri iye anadziŵika kukhala “Mwana wa Davide.” Patsiku la kukwera kwake kwa chilakiko kuloŵa m’Yerusalemu, atakwera pabulu mokwaniritsa ulosi, khamu lochita chidwi la Ayuda limene linamperekeza ndi atumwi ake linafuula mokondwera kuti: “Hosana kwa Mwana wa Davide! Wolemekezeka ndiye wakudza m’dzina la Ambuye, Hosana m’Kumwambamwamba!”—Mateyu 21:9.
“Mwana wa Davide” Ayikidwa pa Mpando Wachifumu Kumwamba
12. Pamene nthaŵi za Akunja zinatha mu 1914, kodi nkuti kumene Kristu, monga woloŵa nyumba wachikhalire wa Davide anaikidwa pa mpando wachifumu?
12 Zaka 2 520 zakuti Akunja aponderezere pansi Ufumu wa Mulungu umene unali mu mzera wa nyumba ya Davide zinatha mu 1914. Pamenepo nthaŵi inafika yakuti Yesu Kristu, “Mwana wa Davide,” aikidwe pampando wachifumu, osati pampando wachifumu wa pansi pano, koma m’miyamba yokwezeka kudzanja lamanja la Yehova Mulungu!—Danieli 7:9, 10, 13, 14.
13. (a) Kodi nkuyambira chaka chiti pamene chaka cha 1914 chinatchulidwa pasadakhale kukhala mapeto a Nthaŵi za Akunja, ndipo ndi ayani? (b) Kodi nchiyani chimene chinali mkhalidwe wa mitundu padziko lapansi kulinga kwa “Mwana wa Davide” woikidwa pampando wachifumu chatsopanoyo?
13 Kuyambira 1876 ndi awo amene anagwirizanitsidwa ndi Watch Tower Bible and Tract Society anasonya mtsogolo ku chaka chosaiŵalika chimenecho. Koma mitundu ya dziko lapansi, ngakhale ya Dziko Lachikristu, inakana kuchivomereza kukhala nthaŵi yakuti iwo atembenuzire maufumu awo a padziko lapansi kwa “Mwana wa Davide” woikidwa pampando wachifumu chatsopanoyo. Iwo sanavomereze kuti iye anali ndi kuyenera kopatsidwa ndi Mulungu kukhala ndi ulamuliro padziko lonse lapansi, limene liri chopondapo mapazi cha Mulungu. (Mateyu 5:35) Iwo anasonyeza kukana kwawo kotheratu Mfumu yoyenererayo mwa kuchita nkhondo ya dziko yoyamba.
-