Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w93 12/15 tsamba 32
  • Mkwiyo Wanga Kapena Thanzi Langa?

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Mkwiyo Wanga Kapena Thanzi Langa?
  • Nsanja ya Olonda—1993
Nsanja ya Olonda—1993
w93 12/15 tsamba 32

Mkwiyo Wanga Kapena Thanzi Langa?

KODI ndani amene samakwiya? Kumachitika kwa tonsefe. Panthaŵi zina mlingo wakutiwakuti wa mkwiyo ungakhale woyenerera. Komatu, kunena zowona, kodi sizowona kuti kaŵirikaŵiri mkwiyo wathu (kapena ukulu wake) umakhala wosayenerera?

Baibulo limatiuza kuti: “Leka kupsa mtima, nutaye mkwiyo: usavutike mtima ungachite choipa.” (Salmo 37:8) Kodi uphungu wotero ngwanzeru motani? Kodi ungayambukire kukhalitsa kwa thanzi lathu?

M’chigawo chake cha “Za Thanzi,” The New York Times inati:

“Anthu amene amakalipakalipa kapena amangokhala amtima wapachala pachinthu chilichonse angakhale akuchita zoipa kwambiri kuposa kudzipangitsa iwo eni kukhala osakondweretsa. Angakhale akudzipha.

“Ofufuza asonkhanitsa umboni wochuluka posachedwapa wosonyeza kuti mkwiyo wosatha ngwovulaza kwambiri kuthupi kwakuti ukuikidwa m’gulu limodzi ndi, ndipo mwinamwake ngakhale kuposa, kusuta fodya, kunenepetsa ndi chakudya cha mafuta ambiri monga wodzetsa imfa ya mwamsanga yaupandu waukulu.

“‘Kufufuza kwathu kukusonyeza kuti udani, mkwiyo wa kukayikira ena ngwofanana ndi maupandu ena a thanzi amene timadziŵa,’ anatero Dr. Redford Williams, wofufuza za mankhwala okhudza mkhalidwe pa Duke University Medical Center.”

Zofufuzidwazo zikusonyeza kuti awo amene amakwiya ndi mavuto a moyo amatulutsa mahomoni ambiri a kupsinjika. Kukalipakalipa kwawo kungachititse kusiyana m’milingo ya cholesterol yotetezera ndi yaupandu, kukumawaika paupandu wa nthenda ya mtima.

Ena anganene kuti, ‘Komatu ndimo mmene ndiliri’ kapena, ‘Ndimmene ndinakulira.’ Komabe, zimenezo sizikutanthauza kuti simungasinthe, mwakuyesayesa mowona mtima kugwiritsira ntchito uphungu wa Mulungu. M’Baibulo lanu, pendani uphungu wake wonena za kukwiya ndi ukali wolembedwa pa Miyambo 14:29, 30; 22:24, 25; Aefeso 4:26; Yakobo 1:19, 20.

Kugwiritsira ntchito nzeru yaumulungu imeneyo kungawongolere thanzi lanu ndi kutalikitsa moyo wanu. Times imeneyo inati: “Ofufuza ambiri anati anthu okwiyakwiya akhoza kuchepetsa kuthekera kwa kufa msanga mwa kusintha mkhalidwe womakwiyakwiyawo.”

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena