-
Yehova Amawerenga ‘Tsitsi Lonse la M’mutu Mwanu’Nsanja ya Olonda—2005 | August 1
-
-
“Sungani Misozi Yanga M’nsupa Yanu”
12. Kodi timadziwa bwanji kuti Yehova amaona mavuto onse amene anthu ake akukumana nawo?
12 Yehova sikuti amangodziwa mtumiki wake aliyense payekha komanso amadziwa bwino lomwe mavuto onse amene amakumana nawo. Mwachitsanzo, Aisrayeli akuzunzidwa kuukapolo, Yehova anauza Mose kuti: “Ndapenyetsetsa mazunzo a anthu anga ali m’Aigupto, ndamvanso kulira kwawo chifukwa cha akuwafulumiza; pakuti ndidziwa zowawitsa zawo.” (Eksodo 3:7) N’zolimbikitsatu kwambiri kudziwa kuti tikamakumana ndi chiyeso chinachake, Yehova amaona ndipo amamva tikamamufuulira kuti atithandize. Ndithu, iye sanyalanyaza mavuto amene tikukumana nawo.
13. Kodi n’chiyani chimasonyeza kuti Yehova amawaganiziradi atumiki ake?
13 Timaonanso kuti Yehova amasamalira anthu amene ali paubwenzi ndi iyeyo poganizira mmene ankamvera poona Aisrayeli akuvutika. Ngakhale kuti iwo ankavutika chifukwa cha kusamva kwawo, Yesaya analemba za Yehova kuti: “M’mazunzo awo onse Iye anazunzidwa.” (Yesaya 63:9) Poti inunso ndinu mtumiki wokhulupirika wa Yehova, musakayikire n’komwe kuti zinazake zikamakupwetekani, Yehovanso zimam’pweteka. Mfundo imeneyitu iyenera kukulimbitsani mtima mukakhala pamavuto ndiponso iyenera kukupatsani mphamvu zotumikira Yehova mmene mungathere.—1 Petro 5:6, 7.
14. Kodi Davide anali pa mavuto otani pamene ankalemba Salmo 56?
14 Mfundo yakuti Mfumu Davide anali wotsimikiza mtima kwambiri kuti Yehova amamuganizira ndiponso kumumvera chisoni akakhala pamavuto imaonekera kwambiri mu Salmo 56. Davide analemba salmo limeneli pamene Mfumu Sauli ankafuna kumupha. Davide anathawira ku Gati, koma Afilisti atamudziwa iye anaopa kuti agwidwa. Davideyo analemba kuti: “Adani anga afuna kundimeza tsiku lonse: pakuti ambiri andithira nkhondo modzikuza.” Chifukwa choti moyo wake unali pachiswe, Davide anapemphera kwa Yehova. Iye anati: “Tsiku lonse atenderuza mawu anga; zolingalira zawo zonse zili pa ine kundichitira choipa.”—Salmo 56:2, 5.
15. (a) Kodi Davide ankatanthauzanji popempha Yehova kuti aike misozi yake m’nsupa kapena kuti ailembe m’buku? (b) Pamene tikukumana ndi mayesero, kodi tisakayikire mfundo yotani?
15 Kenaka, malingana ndi zimene zinalembedwa pa Salmo 56:8, Davide ananena mawu ochititsa chidwi awa: “Muwerenga kuthawathawa kwanga: sungani misozi yanga m’nsupa yanu; kodi siikhala m’buku mwanu?” Awatu ndi mawu ogwira mtima kwambiri osonyeza kuti Yehova amatiganizira kwambiri mwa chikondi chake. Tikakhala pa mavuto tingathe kum’lilira Yehova popemphera. Ngakhale Yesu, yemwe anali munthu wangwiro, anatero. (Ahebri 5:7) Davide sankakayikira ngakhale pang’ono kuti Yehova amaona zovuta zake ndiponso kuti saiwala masautso ake, kungokhala ngati kuti waika misozi yake m’nsupa kapena kuti m’thumba la chikopa ndiponso kuti wailemba m’buku.d Mwina inuyo mumaona kuti misozi yanu ingatsale pang’ono kudzadza thumba limenelo, kapena ingalembedwe m’masamba ambiri zedi a m’bukulo. Ngati mumaona choncho, khazikani mtima pansi. Baibulo limatitsimikizira kuti: “Yehova ali pafupi ndi iwo a mtima wosweka, apulumutsa iwo a mzimu wolapadi.”—Salmo 34:18.
-
-
Yehova Amawerenga ‘Tsitsi Lonse la M’mutu Mwanu’Nsanja ya Olonda—2005 | August 1
-
-
d Kale, nsupa kwenikweni anali matumba a zikopa za nkhosa, mbuzi, ndi ng’ombe omwe ankasungiramo mkaka, batala, tchizi, kapena madzi. Zikopa zofufutidwa bwino anali kuikamo mafuta kapena vinyo.
-