Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Kulemera Kungayese Chikhulupiriro Chanu
    Nsanja ya Olonda—1993 | July 15
    • Potsirizira pake atazindikira kuti kalingaliridwe kake kanali kolakwa, Asafu anati: “Ndikadati, ndidzafotokozera chotere, Taonani, ndikadachita chosakhulupirika ndi mbadwo wa ana ako. Pamene ndinayesa kudziŵitsa ichi, ndinavutika nacho; mpaka ndinaloŵa m’zoyera za Mulungu, ndi kulingalira chitsiriziro chawo. Indedi muwaika poterera: muwagwetsa kuti muwaononge. Ha! m’kamphindi ayesedwa bwinja; athedwa konse ndi zowopsa. Monga anthu atauka, apepula loto; momwemo, Inu Ambuye, pakuuka mudzapeputsa chithunzithunzi chawo.”​—Salmo 73:15-20.

  • Kulemera Kungayese Chikhulupiriro Chanu
    Nsanja ya Olonda—1993 | July 15
    • Asafu anafika pakuzindikira kuti Mulungu anaika oipa “poterera.” Chifukwa chakuti miyoyo yawo inasumikidwa pa zinthu zakuthupi, iwo ali paupandu wakuyang’anizana ndi kugwa kwadzidzidzi. Potsirizira pake, imfa idzawapeza paukalamba, ndipo chuma chawo chopezedwa mosayenera sichidzawatalikitsira moyo wawo. (Salmo 49:6-12) Kulemera kwawo kudzakhala ngati loto losakhalitsa. Chiweruzo cholungama chikhozanso kuwapeza asanakalambe kuti atute zimene anafesa. (Agalatiya 6:7) Popeza kuti afulatira dala Uyo yekha amene akhoza kuwathandiza, iwo ali osoŵa chochita, opanda chiyembekezo. Pamene Yehova achitapo kanthu motsutsana nawo, adzanyansidwa ndi “chithunzithunzi chawo”​—kutchuka kwawo ndi malo awo.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena