Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w01 2/1 tsamba 32
  • “Mitsempha Yako Idzalandirapo Moyo”

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • “Mitsempha Yako Idzalandirapo Moyo”
  • Nsanja ya Olonda—2001
Nsanja ya Olonda—2001
w01 2/1 tsamba 32

“Mitsempha Yako Idzalandirapo Moyo”

PALI chikhulupiriro chakuti matenda ambiri a anthu amayamba chifukwa cha kuvutika m’maganizo koyambitsidwa ndi mantha, chisoni, nsanje, mkwiyo, chidani, ndi kudzimva wamlandu. Poona zimenezi, mawu a m’Baibulo akuti, ‘ukaopa Yehova, . . . mitsempha yako idzalandirapo moyo ndi mafupa ako uwisi,’ n’ngotonthoza zedi!​—Miyambo 3:7, 8.

Mafupa ndiwo nsanamira za thupi. Choncho, Baibulo limagwiritsa ntchito liwu lakuti “mafupa” mwa fanizo kutanthauza munthu weniweniyo, makamaka povutika ndi maganizo osautsa kwambiri. Koma kodi ndi motani mmene kuopa Yehova ‘kungapatsire mitsempha yako moyo’?

Akatswiri a Baibulo, amasiyana maganizo pa mawu akuti “mitsempha” m’ndimeyi. Katswiri wina wothirira ndemanga pa Baibulo ananena kuti, chifukwa chakuti “mitsempha” ndiyo ili “m’katikati mwa thupi,” ingaimirenso ziwalo zonse zofunika kwambiri. Wophunzira Baibulo wina anaganiza kuti liwu lakuti “mitsempha” lingatanthauze mchombo, monga mmene lagwiritsidwira ntchito pa Ezekieli 16:4. Ngati zili choncho, ndiye kuti Miyambo 3:8 ingakhale ikutsimikizira kufunika kwa kudalira Mulungu ndi mtima wonse, monga mmene kakhanda komwe sikanabadwe kamadalira mayi wake pa chilichonse chofunika m’thupi lake. Komabe, maganizo ena n’ngakuti m’vesili, “mitsempha” ikhoza kutanthauza minofu ndi minyewa ya thupi. M’nkhaniyi, mbali zimenezi zingakhale zikulekanitsidwa ndi “mafupa” omwe ndi mbali zolimba za thupi.

Kaya tanthauzo lake lenileni n’lotani, chinthu chimodzi n’chotsimikizika: Kuopa kum’khumudwitsa Yehova ndiyo njira yanzeru. Kutsatira miyezo ya Mulungu kungatipangitse kukhala ndi moyo wabwino tsopano. Kuwonjezera apo, kungachititse kuti Yehova atiyanje, ndipo zimenezi zidzatitsogolera ku moyo wosatha wangwiro​—mwakuthupi ndi mwa maganizo​—m’dziko lake latsopano.​—Yesaya 33:24; Chivumbulutso 21:4; 22:2.

[Mawu a Chithunzi patsamba 32]

Dr. G. Moscoso/​SPL/​Photo Researchers

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena