-
Opani Yehova ndipo Mudzakhala AchimwemweNsanja ya Olonda—1987
-
-
Tcherani Khutu ku Nzeru
Werengani Miyambo 1:1-2:22. “Kuopa Yehova” chiri chofunika chenicheni cha chidziwtso. Ngati tilandira malangizo, sitidzatsagana ndi ochimwa m’kuchita zoipa. Kwa awo owopa Yehova, amawapatsa nzeru imene imawachinjiriza kwa ochita zoipa.
◆ 1:7—Kodi “kuopa Yehova“ nchiyani?
Kuli mantha, ulemu wakuya, ndi kuwopa kwenikweni kwa kusamukondweretsa chifukwa timayamikira ubwino ndi kukoma mtima kwake. “Kuopa Yehova“ kumatanthauza kuvomereza kuti ali Woweruza Wamkulu ndi Wamphamvuyonse, amene alindi kuyenera ndi mphamvu ya kubweretsa chilango kapena Imfa pa osamumvera iye. Chimatanthauzanso kutumikira Mulungu mokhulupirika, kudalira mwa iye kotheratu, ndi kudana ndi chimene chiri ohoipa m’maso mwake.—Masalmo 2:11; 115:11; Miyambo 8:13.
-
-
Opani Yehova ndipo Mudzakhala AchimwemweNsanja ya Olonda—1987
-
-
Phunziro kwa Ife: Ngati tiopa Yehova, tidzalandira malangizo amene iye amapereka kupyolera mu Mawu ake ndi gulu lake. Kulephera kuchita tero kungatiike ife pamodzi ndi “opusa,“ ochimwa opanda umulungu. Chotero tiyeni tliandire malangizo ake achikondi.—Miyambo 1:7; Ahebri 12:6.
-