-
Pezani Nzeru Ndipo Landirani MwamboNsanja ya Olonda—1999 | September 15
-
-
Mawu oyamba a buku la Miyambo, afotokoza cholinga chenicheni cha bukuli: “Miyambo ya Solomo mwana wa Davide, mfumu ya Israyeli. Kudziŵa nzeru ndi mwambo; kuzindikira mawu ozindikiritsa; kulandira mwambo wakusamalira machitidwe, chilungamo, chiweruzo ndi zolunjika; kuchenjeza achibwana, kuphunzitsa mnyamata kudziŵa ndi kulingalira.”—Miyambo 1:1-4.
-
-
Pezani Nzeru Ndipo Landirani MwamboNsanja ya Olonda—1999 | September 15
-
-
Nzeru imaphatikiza mbali zambiri monga kumvetsa, chidziŵitso, kuchenjera, ndi luso la kulingalira. Kumvetsa ndiko kukhoza kuona chimene nkhaniyo ikutanthauza ndi kuzindikira nkhani yonseyo mwa kumvetsa kugwirizana kwa mbali zake zonse ndi mutu wa nkhaniyo, potero mukumamvetsa tanthauzo lake. Chidziŵitso chimafuna kudziŵa ndi kumvetsa chifukwa chake kuchita zinthu zina zake n’kwabwino kapena ayi. Mwachitsanzo, munthu womvetsa angazindikire pamene winawake akufuna kulakwa, ndipo nthaŵi yomweyo angam’chenjeze za kuwopsa kwa chomwe akufuna kuchitacho. Koma adzafunikira chidziŵitso kuti azindikire chifukwa chake munthu ameneyo akuchitira zimenezo kuti athe kupeza njira yabwino yom’pulumutsira.
-