Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Buku Lothandiza pa Moyo Wamakono
    Buku la Anthu Onse
    • Koma ulamuliro wa makolo​—‘nthyole yolangira’—​suyenera kukhala wankhanza.b (Miyambo 22:15; 29:15) Baibulo limachenjeza makolo kuti: “Musamawawongolera mopambanitsa ana anu, kuti mungawatayitse mtima.” (Akolose 3:​21, Phillips) Limavomerezanso kuti nthaŵi zambiri kulanga mwana mwa kumkwapula sindiko njira yothandiza kwambiri yomphunzitsira. Miyambo 17:10 imati: “Chidzudzulo chiloŵa mkati mwa wozindikira, kopambana ndi kukwapula wopusa kwambiri.” Ndiponso, Baibulo limalimbikitsa chilango choteteza. Pa Deuteronomo 11:19 makolo akulimbikitsidwa kugwiritsira ntchito mpata wa nthaŵi yocheza kukhomereza mwa ana awo makhalidwe abwino.​—Onaninso Deuteronomo 6:6, 7.

  • Buku Lothandiza pa Moyo Wamakono
    Buku la Anthu Onse
    • b M’nthaŵi za m’Baibulo, liwulo “nthyole” (Chihebri, sheʹvet) linali kutanthauza “mtengo” kapena “ndodo,” ngati ija imene mbusa amagwiritsira ntchito.10 Pano, nthyole ya ulamuliro ikutanthauza kulangiza mwachikondi, osati nkhanza yokhaulitsa ayi.​—Yerekezerani ndi Salmo 23:4.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena