-
Buku Lothandiza pa Moyo WamakonoBuku la Anthu Onse
-
-
Koma ulamuliro wa makolo—‘nthyole yolangira’—suyenera kukhala wankhanza.b (Miyambo 22:15; 29:15) Baibulo limachenjeza makolo kuti: “Musamawawongolera mopambanitsa ana anu, kuti mungawatayitse mtima.” (Akolose 3:21, Phillips) Limavomerezanso kuti nthaŵi zambiri kulanga mwana mwa kumkwapula sindiko njira yothandiza kwambiri yomphunzitsira. Miyambo 17:10 imati: “Chidzudzulo chiloŵa mkati mwa wozindikira, kopambana ndi kukwapula wopusa kwambiri.” Ndiponso, Baibulo limalimbikitsa chilango choteteza. Pa Deuteronomo 11:19 makolo akulimbikitsidwa kugwiritsira ntchito mpata wa nthaŵi yocheza kukhomereza mwa ana awo makhalidwe abwino.—Onaninso Deuteronomo 6:6, 7.
-
-
Buku Lothandiza pa Moyo WamakonoBuku la Anthu Onse
-
-
b M’nthaŵi za m’Baibulo, liwulo “nthyole” (Chihebri, sheʹvet) linali kutanthauza “mtengo” kapena “ndodo,” ngati ija imene mbusa amagwiritsira ntchito.10 Pano, nthyole ya ulamuliro ikutanthauza kulangiza mwachikondi, osati nkhanza yokhaulitsa ayi.—Yerekezerani ndi Salmo 23:4.
-