-
Buku Lothandiza pa Moyo WamakonoBuku la Anthu Onse
-
-
Thanzi la munthu nthaŵi zambiri limakhudzidwa ndi mkhalidwe wa maganizo ake ndi mtima wake. Mwachitsanzo, asayansi pakufufuza kwawo apeza kuti mkwiyo umakhala ndi zotsatira zake zoipa. “Umboni wochuluka womwe ulipo ukusonyeza kuti anthu amene amakwiya msanga ali pangozi yaikulu yodwala nthenda ya mtima (ndi matenda enanso) chifukwa cha zinthu zosiyanasiyana, kuphatikizapo kusoŵa mabwenzi, kusokonezeka kwa zinthu m’thupi atakwiya, ndi kuchita zinthu zambiri zangozi pa thanzi lawo,” akutero Dr. Redford Williams, Director of Behavioral Research pa Duke University Medical Center, ndi mkazi wake, Virginia Williams, m’buku lawo lakuti Anger Kills.13
Zaka zikwi zambiri asayansi asanafufuze zimenezo, Baibulo, ndi mawu apafupi koma omveka, linasonyeza kuti pali kugwirizana pakati pa mkhalidwe wa mtima wathu ndi thanzi lathu: “Mtima wabwino ndi moyo wa thupi; koma nsanje ivunditsa mafupa.” (Miyambo 14:30; 17:22) Mwanzeru, Baibulo linalangiza kuti: “Leka kupsa mtima, nutaye mkwiyo” ndi kuti, “Usakangaze mumtima mwako kukwiya.”—Salmo 37:8; Mlaliki 7:9.
-
-
Buku Lothandiza pa Moyo WamakonoBuku la Anthu Onse
-
-
“Usafulumire kusonyeza mkwiyo; pakuti zitsiru ndizo zimasunga mkwiyo.” (Mlaliki 7:9, The New English Bible) Nthaŵi zambiri mkwiyo ndiwo umayamba munthu asanachite kanthu. Munthu wofulumira kukwiya ngwopusa, chifukwa zimenezo zingampangitse kulankhula kapena kuchita kanthu kena mwansontho.
-