-
Kodi Mudzanena Kuti,“Ndine Pano! Munditumize Ine”?Nsanja ya Olonda—1987
-
-
10. (a) Kodi vuto linali pati m’kukhala kwa anthuwo monga akhungu ndi ogontha? (b) Nchiyani chimene Yesaya anatanthauza mwa kufunsa kuti, “Kufikira liti?”
10 Kulakwa kunali ndi anthuwo. Mosasamala kanthu za kuwalola kwa Yesaya kuti “amve,” iwo sakatenga chidziŵitso kapena kupeza kuzindikira. Mulungu ananeneratu pasadakhale kuti ambiri, chifukwa cha kuuma khosi kwawo ndi kawonedwe kawo kopanda uzimu, sadzavomereza. Ochepa koposa angadzatero. Koma ochulukira adzakhala monga akhungu monga ngati maso awo anatsekedwa ndi utoto wamphamvu koposa, ngati mungalingalire chimenecho. Ndi kuutali wotani kumene mkhalidwe woipa umenewu ukapitirira? Chimenecho, m’malo mwa kutchula ndi zaka zingati zimene iye adzatumikira, ndi chimene Yesaya anafunsa ndi mawu awa: “Mpaka liti, Yehova?” Mulungu anayankha: “Mpaka midzi ikhala bwinja, yopanda wokhalamo.” Ndipo chotero chinachitika, ngakhale kuti pambuyo pa nthaŵi ya moyo ya Yesaya. Ababulo anachotsa anthu a padziko lapansi, kusiya Yuda “wosakazidwa kukhala bwinja.”—Yesaya 6:11, 12; 2 Mafumu 25:1-26.
-
-
Kodi Mudzanena Kuti,“Ndine Pano! Munditumize Ine”?Nsanja ya Olonda—1987
-
-
12. Ndi maziko a m’Malemba otani amene alipo a kuitanira Yesu monga Yesaya Wamkulu?
12 Zaka mazana angapo pambuyo pa imfa ya Yesaya, wina anabwera amene tingamutche Yesaya Wamkulu—Yesu Kristu. Mu kukhalapo kwake asanakhale munthu, iye anadzipereka kutumizidwa ndi Atate wake kudziko lapansi, kumene iye akaphatikiza m’kulalikira kwake zinthu zimene Yesaya analemba. (Miyambo 8:30, 31; Yohane 3:17, 34; 5:36-38; 7:28; 8:42; Luka 4:16-19; Yesaya 61:1) Mwachindunji kwambiri, Yesu anadziphatikiza iyemwini ndi Yesaya mutu 6 pamene anali kulongosola chifukwa chimene Iye anaphunzitsira monga mmene Anachitira. (Mateyu 13:10-15; Marko 4:10-12; Luka 8:9, 10) Chimenecho chinali choyenera, popeza Ayuda ambiri omwe anamva Yesu sanali ofunitsitsa kulandira uthenga wake ndi kuchita pa iwo monga mmene awo amene anamva mneneri Yesaya sanali ofunitsitsa kulandira uthenga wake. (Yohane 12:36-43) Ndiponso, mu 70 C.E. Ayuda omwe anadzipanga iwo eni kukhala ‘akhungu ndi ogontha’ ku uthenga wa Yesu anakumana ndi chiwonongeko chofanana ndi chija cha mu 607 B.C.E. Chochitika chimenechi mu zana loyamba chinali chisautso pa Yerusalemu ‘chonga chimene sichidakhale chotero kuyambira chiyambi cha dziko lapansi ndipo sichidzachitikanso.’ (Mateyu 24:21) Komabe, monga mmene Yesaya ananeneratu, otsalira, kapena “mbewu yopatulika,” anasonyeza chikhulupiriro. Awa anapangidwa kukhala mtundu wauzimu, “Israyeli wodzozedwa wa Mulungu.”—Agalatiya 6:16.
13. Nchifukwa ninji tingayembekezere kukwaniritsidwa kwina kwa Yesaya mutu 6?
13 Tsopano tifika ku kukwaniritsidwa kwina kozikidwa pa Baibulo kwa Yesaya mutu 6. Monga mfungulo kukumvetsetsa ichi, lingalirani mawu a mtumwi Paulo chifupifupi chaka cha 60 C.E. Iye analongosola chifukwa chimene Ayuda amene anamva iye mu Roma sakanalandira “umboni wake ponena za ufumu wa Mulungu.” Chifukwa chake chinali chakuti Yesaya 6:9, 10 anali kukwaniritsidwanso. (Machitidwe 28:17-27) Kodi ichi chikutanthauza kuti pambuyo pa kuchoka kwa Yesu pa chiwonetsero cha dziko lapansi, ophunzira ake odzozedwa anayenera kupitiriza ntchito yofanana ndi ya Yesaya? Inde, ndithudi!
14. Ndimotani mmene ophunzira a Yesu anayenera kuchitira ntchito yonga ya Yesaya?
14 Yesaya Wamkuluyo asanakwere kumwamba, ananena kuti ophunzira ake adzalandira mzimu woyera ndipo pambuyo pa chimenecho “adzakhala mboni za [iye] ponse paŵiri m’Yerusalemu ndi m’Yudeya monse ndi m’Samariya ndi kufikira malekezero ake adziko.” (Machitidwe 1:8) Mofanana ndi mmene guwa loperekerapo nsembe linaperekera chimene chinafunikira kaamba ka kuchotsa zolakwa za Yesaya, mofananamo nsembe ya Yesu inali maziko kaamba ka ophunzira ake kukhala ndi ‘machimo awo atakhululukidwa.’ (Levitiko 6:12, 13; Ahebri 10:5-10; 13:10-15) Chotero, Mulungu akawadzoza iwo ndi mzimu woyera, womwe ukawapatsanso iwo mphamvu kukhala ‘mboni ku malekezero a dziko lapansi.’ Ponse paŵiri mneneri Yesaya ndi Yesaya Wamkulu anatumizidwa kulengeza uthenga wa Mulungu. Mofananamo, atsatiri odzozedwa a Yesu “anatumizidwa kuchokera kwa Mulungu . . . m’chigwirizano ndi Kristu.”—2 Akorinto 2:17.
15. Nchiyani chimene chakhala yankho la chisawawa ku kulalikira konga kunja kwa Yesaya m’nthaŵi yathu, kuloza ku m’tsogolo motani?
15 M’nthaŵi zamakono, makamaka kuyambira pa mapeto a Nkhondo ya Dziko I, Akristu odzozedwa awona kufunika kwa kulengeza uthenga wa Mulungu. Ichi chimaphatikizapo nsonga yotonthoza yakuti “tsiku la kubwezera la Mulungu wathu” liri pafupi. (Yesaya 61:2) Kusakaza kwake kudzakhala nkhonya makamaka kwa Dziko la Chipembedzo, limene kwanthaŵi yaitali ladzinenera kukhala anthu a Mulungu, monga mmene anachitira Israyeli wakale. Mosasamala kanthu za zaka makumi angapo a kulalikira kokhulupirika kwa mboni zodzozedwa za Mulungu, ambiri m’Dziko la Chipembedzo ‘alemeretsa mitima yawo ndi kutseka makutu awo; ndi maso awo atsekedwa.’ Ulosi wa Yesaya umasonyeza kuti ichi chidzapitiriza kukhala tero “kufikira midzi idzakhala bwinja, yopanda wokhalamo, ndi nyumba zopanda anthu ndi dziko likhala bwinja ndithu.” Ichi chidzasonyeza kutha kwa dongosolo loipa la zinthu iri.—Yesaya 6:10-12.
-