Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Kubwezeretsedwa kwa Munda wa Edene—Padziko Lonse Lapansi
    Chisungiko cha Padziko Lonse mu Ulamuliro wa “Kalonga wa Mtendere”
    • 6, 7. (a) Kodi nchifukwa ninji zinyama sizidzakhala chiwopsezo chirichonse kwa anthu? (b) Kodi ndiulosi wotani pa mfundoyi umene udzakwaniritsidwa kwenikweni?

      6 Zolengedwa zanyama sizidzavulaza kapena kuwopseza nzika za Paradaiso wobwezeretsedwanso. Mulungu adzabwezeretsa mlingo uliwonse wotayika wa kuwopa anthu. Motero tingayembekezere kuti malongosoledwe okondweretsa onena za nyama operekedwa pa Yesaya 11:6-9 akakhala ndi kukwaniritsidwa kwenikweni mkati mwa Kulamulira kwa Zaka Chikwi kwa “Kalonga wa Mtendere” kuti:

      7 “Mmbulu udzakhala pamodzi ndi mwana wankhosa, ndipo nyalugwe adzagona pansi ndi mwana wa mbuzi; ndipo mwana wang’ombe ndi mwana wa mkango ndi choŵeta chonenepa pamodzi; ndipo mwana wamng’ono adzazitsogolera. Ndipo ng’ombe yaikazi ndi chirombo zidzadya pamodzi; ndipo ana awo aang’ono adzagona pansi; ndipo mkango udzadya udzu ngati ng’ombe. Ndipo mwana wakuyamwa adzaseŵera pa una wa mamba, ndi mwana woleka kuyamwa adzaika dzanja lake m’funkha la mphiri. Sizidzaipitsa, sizidzasakaza m’phiri langa lonse loyera, chifukwa kuti dziko lapansi lidzadzala ndi odziŵa Yehova, monga madzi adzaza nyanja.”

      8. Kodi nchiyani chimene chikutanthauzidwa mwa mawu olosera akutiwo fumbi lidzakhala ‘chakudya cha njoka’?

      8 Kukakhala kusanena chimodzi kuti Mulungu auzire ulosi wotere kukhala ndi tanthauzo lauzimu lokha ndipo osati kusonyeza zinthu zotere m’moyo weniweni wa padziko lapansi. Mofananamo, Yesaya 65:25 amatiuza kuti: “Mmbulu ndi mwana wa nkhosa zidzadya pamodzi; ndi mkango udzadya udzu ngati ng’ombe; ndi fumbi lidzakhala chakudya cha njoka.” Kodi zimenezi zikusonyeza kusolotsedwa kwa njoka pambulumbwa yonse munda wa Edene? Ayi, mawu aulosi akuti “fumbi lidzakhala chakudya cha njoka amatathauza kuti zirombo zokwaŵa sizidzakhalanso chiwopsezo kumoyo ndi kuthanzi labwino la zolengedwa zaumunthu. Zidzafunikira kuvomereza kuti anthu ali mbuye wawo amene ali ndi ulamuliro pa chirichonse chamoyo padziko lapansi, monga momwedi zinaliri ndi Adamu m’munda wa Edene pamene anatcha nyama zonse maina popanda kuchita mantha.—Genesis 2:19, 20; Hoseya 2:18.

  • Kubwezeretsedwa kwa Munda wa Edene—Padziko Lonse Lapansi
    Chisungiko cha Padziko Lonse mu Ulamuliro wa “Kalonga wa Mtendere”
    • 11. Kodi ndimasinthidwe otani achinenero amene adzachitika, ndipo kodi zimenezi zidzayambukira anthu motani?

      11 Kodi Paradaiso wa padziko lonse lapansi adzakanthidwa ndi chisokonezo cha kukhala ndi zinenero zambiri? Ayi, chifukwa chakuti “Kalonga wa Mtendere” akunenedwanso kukhala “Mulungu Wamphamvu.” (Yesaya 9:6) Motero iye ali wokhoza kuthetsa chisokonezo cha chinenero chimene chinayambira pa Nsanja ya Babele. (Genesis 11:6-9) Kodi nchiti chimene chidzakhala chinenero cha ana onse a padziko lapansi a “Atate Wosatha”? Kodi chidzakhala chinenero choyambirira cha Adamu woyamba, chimene Yehova anampatsa? Mwinamwake. Mulimonse mmene ziti zidzakhalire, zopinga zonse za chinenero zidzathetsedwa. Mudzakhoza kudzayenda ulendo kulikonse ndi kulankhula ndi anthu. Mudzakhoza kuwamva, ndipo iwo adzakhoza kukumvani. Padzakhala chinenero chimodzi kaamba ka anthu onse, ndipo kudzakhala koyenerera kuti Baibulo lathunthu lipezeke m’chinenero chimenecho. (Yerekezerani ndi Zefaniya 3:9.) M’chinenero chimenecho dziko lonse lapansi lidzadzazidwa ndi kudziŵa Yehova “monga madzi adzaza nyanja.”—Yesaya 11:9.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena