-
Alanditsidwa ku Mano a Mikango!Samalani Ulosi wa Danieli!
-
-
20. Kodi n’chiyani chinachitikira adani a Danieli adumbowo?
20 Danieli tsopano anali pabwino, koma Dariyo anali ndi ntchito ina yoti achite. “Italamulira mfumu, anabwera nawo amuna aja adam’neneza Danieli, nawaponya m’dzenje la mikango, iwowa, ana awo, ndi akazi awo; ndipo asanafike pansi pa dzenje mikango inawaposa mphamvu, niphwanya mafupa awo onse.”d—Danieli 6:24.
21. Pochita ndi apabanja la anthu olakwa, kodi panali kusiyana kotani pakati pa Chilamulo cha Mose ndi malamulo a mitundu ina ya m’nthaŵi zakale?
21 Zikuoneka kuti inali nkhanza yoipitsitsa kuphera limodzi akazi awo ndi ana awo a anthu achiwembuwo. Mosiyana ndi zimene zinachitikazo, Chilamulo chimene Mulungu anapereka kudzera mwa mneneri wake Mose chinati: “Atate asaphedwere ana, ndi ana asaphedwere atate; munthu yense aphedwere tchimo lakelake.” (Deuteronomo 24:16) Komabe, m’mitundu ina ya m’nthaŵi zakale, sikunali kwachilendo kunyonga wochimwayo limodzi ndi apabanja lake, ngati cholakwacho chinali chachikulu kwambiri. Mwina anachita zimenezo poopera kuti apabanjawo angadzafune kubwezera panthaŵi ina. Komabe, chenicheni n’chakuti si Danieli anachititsa kuphedwa kwa mabanja a akuluakulu ndi akalongawo. Mwachidziŵikire, iye anamva chisoni kaamba ka tsoka limene amuna oipa amenewo anadzetsa pamabanja awo.
-
-
Alanditsidwa ku Mano a Mikango!Samalani Ulosi wa Danieli!
-
-
d Liwu lakuti “adam’neneza” linatembenuzidwa kuchokera ku mawu achialamu amene angatembenuzidwenso kuti “anam’dyera miseche.” Izi zikusonyeza cholinga chadumbo cha adani a Danieli.
-