Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Ufumu Ukulamulira
    Nsanja ya Olonda (Yophunzira)—2022 | July
    • 10. (a) Kodi timaona zinthu ziti mu ulamuliro wa Britain ndi America zomwe ulosi wa Danieli unaneneratu? (b) Kodi tiyenera kusamala ndi chiyani? (Onani bokosi lakuti, “Samalani ndi Dongo.”)

      10 Choyamba, mosiyana ndi maulamuliro ena amphamvu padziko lonse otchulidwa m’masomphenyawa, ulamuliro wa Britain ndi America sukuimiridwa ndi zinthu zolimba ngati golide kapena siliva, koma chitsulo chosakanizika ndi dongo. Dongolo likuimira “ana a anthu” kapena kuti anthu wamba. (Dan. 2:43) Monga mmene timaonera masiku ano, zochita za anthu pa nkhani ya zisankho, ziwonetsero, kumenyera maufulu komanso kukhazikitsa mabungwe zimachititsa kuti ulamuliro womalizawu uzivutika kukwaniritsa zolinga zake.

      Samalani ndi Dongo

      Mapazi a chitsulo ndi dongo a chifaniziro chachikulu chomwe Danieli anaona m’masomphenya. Pakati pa mapaziwo pakuoneka opanga zionetsero omwe akuyambitsa zipolowe, asilikali ali ndi zishango, atsogoleri a mayiko akumana pamodzi komanso mamembala a bungwe la United Nations ali pamsonkhano.

      Mu ulosi wa Danieli, dongo lomwe lili kumapazi a chifaniziro limaimira anthu wamba. Iwo amakhala ndi mphamvu pa atsogoleri a ndale komanso ulamuliro wawo. (Dan. 2:41-43) Kodi zimenezi zingakhale zoopsa kwa ife? Inde. Ngati sitingateteze mtima wathu, tikhoza kuyamba kukhala kumbali ya dziko. Mwachitsanzo tikhoza kuyamba kutengeka ndi maganizo a anthu omwe amafuna kusintha zinthu pochita zionetsero kapena zandale. (Miy. 4:23; 24:21) Kodi tingapewe bwanji msampha umenewu? Tizikumbukira kuti Satana ndi amene akulamulira dzikoli. (1 Yoh. 5:19) Ndipo Ufumu wa Mulungu wokha ndi umene tiyenera kuuyembekezera.​—Sal. 146:3-5.

  • Ufumu Ukulamulira
    Nsanja ya Olonda (Yophunzira)—2022 | July
    • Samalani ndi Dongo

      Mapazi a chitsulo ndi dongo a chifaniziro chachikulu chomwe Danieli anaona m’masomphenya. Pakati pa mapaziwo pakuoneka opanga zionetsero omwe akuyambitsa zipolowe, asilikali ali ndi zishango, atsogoleri a mayiko akumana pamodzi komanso mamembala a bungwe la United Nations ali pamsonkhano.

      Mu ulosi wa Danieli, dongo lomwe lili kumapazi a chifaniziro limaimira anthu wamba. Iwo amakhala ndi mphamvu pa atsogoleri a ndale komanso ulamuliro wawo. (Dan. 2:41-43) Kodi zimenezi zingakhale zoopsa kwa ife? Inde. Ngati sitingateteze mtima wathu, tikhoza kuyamba kukhala kumbali ya dziko. Mwachitsanzo tikhoza kuyamba kutengeka ndi maganizo a anthu omwe amafuna kusintha zinthu pochita zionetsero kapena zandale. (Miy. 4:23; 24:21) Kodi tingapewe bwanji msampha umenewu? Tizikumbukira kuti Satana ndi amene akulamulira dzikoli. (1 Yoh. 5:19) Ndipo Ufumu wa Mulungu wokha ndi umene tiyenera kuuyembekezera.​—Sal. 146:3-5.

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena