-
Kodi Ufumu wa Mulungu N’chiyani?Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
-
-
Uthenga wofunika kwambiri m’Baibulo ndi wokhudza Ufumu wa Mulungu. Yehova adzagwiritsa ntchito Ufumu umenewu pokwaniritsa cholinga chimene anali nacho chokhudza dziko lapansili. Ndiye kodi Ufumu wa Mulungu ndi chiyani? Timadziwa bwanji kuti Ufumuwu ukulamulira panopa? Ndi zinthu ziti zimene Ufumuwu wachita kale? Nanga udzachita zotani kutsogoloku? Mafunsowa ayankhidwa m’phunziroli komanso maphunziro awiri otsatira.
1. Kodi Ufumu wa Mulungu n’chiyani, nanga Mfumu yake ndi ndani?
Ufumu wa Mulungu ndi boma limene linakhazikitsidwa ndi Yehova Mulungu. Mfumu yake ndi Yesu Khristu ndipo akulamulira kuchokera kumwamba. (Mateyu 4:17; Yohane 18:36) Ponena za Yesu, Baibulo limati: “Iye adzalamulira monga Mfumu . . . kwamuyaya.” (Luka 1:32, 33) Monga Mfumu ya Ufumu wa Mulungu, Yesu adzalamulira anthu onse padzikoli.
2. Kodi ndi ndani akulamulira ndi Yesu?
Yesu sakulamulira yekha. Anthu ochokera “mu fuko lililonse, chinenero chilichonse, mtundu uliwonse, ndi dziko lililonse . . . adzakhala mafumu olamulira dziko lapansi.” (Chivumbulutso 5:9, 10) Ndi anthu angati amene adzalamulire ndi Khristu? Kungoyambira pamene Yesu anabwera padziko lapansi, anthu ambiri akhala otsatira ake ndipo panopa alipo mamiliyoni ambiri. Koma ndi anthu okwana 144,000 okha amene adzapite kumwamba kukalamulira ndi Yesu. (Werengani Chivumbulutso 14:1-4.) Koma Akhristu ena onse adzakhala padziko lapansi ndipo azidzalamuliridwa ndi Ufumu wa Mulungu.—Salimo 37:29.
3. Kodi Ufumu wa Mulungu umaposa bwanji maboma a anthu?
Ngakhale olamulira a dzikoli atayesetsa bwanji kuchita zinthu zabwino, iwo sangakwanitse kuchita zonse zimene akufuna. Pakapita nthawi amalowedwa m’malo ndi olamulira ena odzikonda kwambiri omwe safuna kuthandiza anthu. Mosiyana ndi olamulira amenewa, Yesu yemwe ndi Mfumu ya Ufumu wa Mulungu sadzalowedwa m’malo ndi wina aliyense. Mulungu wakhazikitsa “ufumu umene sudzawonongedwa ku nthawi zonse.” (Danieli 2:44) Yesu adzalamulira dziko lonse lapansi ndipo sazidzakondera mtundu winawake wa anthu. Yesu ndi wachikondi, wachifundo komanso wachilungamo ndipo adzaphunzitsa anthu kuti azidzasonyezana makhalidwe amenewa.—Werengani Yesaya 11:9.
FUFUZANI MOZAMA
Fufuzani kuti mudziwe chifukwa chake Ufumu wa Mulungu uli wabwino kwambiri kuposa maboma a anthu.
4. Ufumu wa Mulungu udzalamulira dziko lonse lapansi
Yesu Khristu ali ndi mphamvu zolamulira dzikoli kuposa anthu onse amene akulamulira dzikoli. Werengani Mateyu 28:18, kenako mukambirane funso ili:
Kodi ulamuliro wa Yesu umaposa bwanji ulamuliro wa anthu?
Maboma a anthu amasinthasintha ndipo dziko lililonse limakhala ndi wolamulira wake. Nanga bwanji Ufumu wa Mulungu? Werengani Danieli 7:14, kenako mukambirane mafunso awa:
Popeza Ufumu wa Mulungu “sudzawonongedwa,” kodi zimenezi zili ndi ubwino wotani?
Kodi mukuganiza kuti tidzapindula bwanji Ufumu wa Mulungu ukamadzalamulira dziko lonse?
5. Maboma a anthu ayenera kuchotsedwa
N’chifukwa chiyani Ufumu wa Mulungu uyenera kulowa m’malo mwa maboma a anthu? Onerani VIDIYO, kenako mukambirane funso lotsatirali:
Kodi zotsatira za ulamuliro wa anthu ndi zotani?
Werengani Mlaliki 8:9, kenako mukambirane mafunso awa:
Kodi mukuona kuti n’zoyenera kuti Ufumu wa Mulungu udzalowe m’malo mwa maboma a anthu? N’chifukwa chiyani mukutero?
6. Ufumu wa Mulungu uli ndi olamulira amene amatimvetsa
Popeza Yesu, yemwe ndi Mfumu yathu anakhalapo munthu, iye ‘amatimvera chisoni pa zofooka zathu.’ (Aheberi 4:15) Yehova anasankha amuna ndi akazi okwana 144,000 omwe adzalamulire ndi Yesu kuchokera “mu fuko lililonse, chinenero chilichonse, mtundu uliwonse, ndi dziko lililonse.”—Chivumbulutso 5:9.
Popeza kuti Yesu komanso onse amene adzalamulire naye anakhalapo anthu, kodi mukuona kuti zimenezi n’zolimbikitsa? N’chifukwa chiyani mukutero?
Yehova wakhala akusankha amuna ndi akazi ochokera m’mitundu yosiyanasiyana kuti adzalamulire ndi Yesu
7. Ufumu wa Mulungu uli ndi malamulo abwino kwambiri
Maboma a anthu amapanga malamulo omwe amayenera kuthandiza ndi kuteteza nzika zawo. Nawonso Ufumu wa Mulungu uli ndi malamulo amene nzika zake zimayenera kuwatsatira. Werengani 1 Akorinto 6:9-11, kenako mukambirane mafunso awa:
Kodi mukuganiza kuti zinthu zidzakhala bwanji padzikoli aliyense akamadzatsatira malamulo a Mulungu?a
Yehova amayembekezera kuti nzika za Ufumu wake zizitsatira malamulo ake, kodi mukuganiza kuti zimene Yehova amafunazi n’zoyenera? N’chifukwa chiyani mukutero?
Ndi mfundo iti imene ikusonyeza kuti anthu amene satsatira malamulo amenewa atha kusintha?—Onani vesi 11.
Maboma amakhazikitsa malamulo n’cholinga chofuna kuthandiza ndi kuteteza nzika zawo. Ufumu wa Mulungu uli ndi malamulo abwino kwambiri omwe amathandiza ndi kuteteza nzika zake
MUNTHU WINA ANGAKUFUNSENI KUTI: “Kodi Ufumu wa Mulungu n’chiyani?”
Kodi mungamuyankhe bwanji?
ZOMWE TAPHUNZIRA
Ufumu wa Mulungu ndi boma lomwe lili kumwamba ndipo udzalamulira dziko lonse lapansi.
Kubwereza
Kodi ndi ndani amene adzalamulire mu Ufumu wa Mulungu?
Kodi Ufumu wa Mulungu umaposa bwanji maboma a anthu?
Kodi Yehova amayembekezera kuti nzika za Ufumu wake zizichita chiyani?
ONANI ZINANSO
Onani zimene Yesu anaphunzitsa zokhudza komwe Ufumu wa Mulungu uli.
“Kodi Ufumu wa Mulungu Uli Mumtima Mwanu?” (Nkhani yapawebusaiti)
N’chifukwa chiyani a Mboni za Yehova amaona kuti kukhala okhulupirika ku Ufumu wa Mulungu n’kofunika kwambiri kuposa kukhala okhulupirika ku maulamuliro a anthu?
Onani zomwe Baibulo limafotokoza zokhudza anthu 144,000 omwe Yehova amawasankha kuti adzalamulire ndi Yesu.
“Kodi Ndi Ndani Amene Amapita Kumwamba?” (Nkhani yapawebusaiti)
N’chiyani chinathandiza mayi wina yemwe anali m’ndende kukhulupirira kuti Mulungu yekha ndi amene angabweretse chilungamo padzikoli?
“Kumene Ndinadziwira Yemwe Adzathetse Kupanda Chilungamo” (Galamukani!, November 2011)
-
-
Kodi Ufumu wa Mulungu Udzachita Zotani?Mungakhale Ndi Moyo Mpaka Kalekale—Kuphunzira Baibulo Mokambirana
-
-
Ufumu wa Mulungu unayamba kale kulamulira. Posachedwapa Ufumuwu ubweretsa madalitso ambiri padzikoli. Tiyeni tione ena mwa madalitso amene tidzasangalale nawo Ufumuwu ukadzayamba kulamulira dziko lonse lapansi.
1. Kodi Ufumu wa Mulungu udzachita chiyani kuti ubweretse mtendere ndi chilungamo padzikoli?
Yesu yemwe ndi Mfumu ya Ufumu wa Mulungu, adzawononga anthu oipa ndi maboma onse a anthu pa nkhondo ya Aramagedo. (Chivumbulutso 16:14, 16) Pa nthawi imeneyo, tidzaona kukwaniritsidwa kwa lonjezo la m’Baibulo ili: “Patsala kanthawi kochepa, woipa sadzakhalakonso.” (Salimo 37:10) Yesu adzagwiritsa ntchito Ufumuwu pobweretsa mtendere komanso chilungamo padziko lonse lapansi.—Werengani Yesaya 11:4.
2. Kodi moyo udzakhala wotani chifuniro cha Mulungu chikadzachitika padziko lapansi?
Ufumu wa Mulungu ukamadzalamulira dzikoli, “olungama adzalandira dziko lapansi, ndipo adzakhala mmenemo kwamuyaya.” (Salimo 37:29) Zidzakhala zosangalatsa kwambiri kuona kuti aliyense padzikoli ndi wolungama ndipo akukonda Yehova ndi anthu ena. Palibe aliyense amene azidzadwala ndipo anthu onse adzakhala ndi moyo mpaka kalekale.
3. Kodi Ufumu wa Mulungu udzachita zotani anthu oipa akadzawonongedwa?
Anthu oipa akadzawonongedwa, Yesu adzalamulira monga Mfumu kwa zaka 1,000. Pa nthawiyi, Yesu ndi olamulira anzake okwana 144,000, adzathandiza anthu onse padzikoli kuti akhale angwiro. Pofika kumapeto kwa zaka 1,000, dziko lonse lidzakhala paradaiso ndipo anthu azidzakhala mosangalala chifukwa chomvera malamulo a Yehova. Kenako Yesu adzabwezera Ufumu kwa Atate wake Yehova. Pa nthawi imeneyo, dzina la Yehova ‘lidzayeretsedwa’ kusiyana ndi kale lonse. (Mateyu 6:9, 10) Aliyense adzadziwa kuti Yehova ndi wolamulira wabwino kwambiri yemwe amaganizira atumiki ake. Kenako Yehova adzawononga Satana, ziwanda ndi anthu onse amene adzasonyeze kuti sakufuna kumvera ulamuliro wake. (Chivumbulutso 20:7-10) Zimenezi zikadzachitika, madalitso amene Ufumu wa Mulungu udzabweretse padzikoli adzakhalapo mpaka kalekale.
FUFUZANI MOZAMA
Fufuzani kuti mudziwe chifukwa chake sitikayikira kuti Mulungu adzagwiritsa ntchito Ufumu wake pokwaniritsa malonjezo onse amene ali m’Baibulo.
4. Mulungu adzathetsa maboma onse a anthu
Baibulo limati: “Munthu wapweteka munthu mnzake pomulamulira.” (Mlaliki 8:9) Yehova adzagwiritsa ntchito Ufumu wake pothetsa zinthu zonse zopanda chilungamo zimene anthu amachitira anzawo.
Werengani Danieli 2:44 ndi 2 Atesalonika 1:6-8, kenako mukambirane mafunso awa:
Kodi Yehova komanso mwana wake Yesu, adzachita chiyani ndi maboma a anthu komanso anthu amene amawatsatira?
Kodi zimene mwaphunzira zokhudza Yehova ndi Yesu zikukutsimikizirani bwanji kuti azidzachita zinthu mwachilungamo?
5. Yesu ndi Mfumu yabwino kwambiri
Monga Mfumu ya Ufumu wa Mulungu, Yesu adzachitira anthu zinthu zabwino kwambiri padzikoli. Onerani VIDIYO kuti muone umboni wosonyeza kuti Yesu ndi wofunitsitsa kuthandiza anthu komanso kuti Mulungu anamupatsa mphamvu zochitira zimenezo.
Zimene Yesu ankachita ali padzikoli, zinasonyeza zimene Ufumu wa Mulungu udzachitire anthu padzikoli. Pa madalitso amene ali m’munsiwa, ndi dalitso liti limene inuyo mukuliyembekezera kwambiri? Werengani malemba amene ali kutsogolo kwa dalitso lililonse.
ALI PADZIKOLI, YESU . . .
ALI KUMWAMBA, YESU . . .
anathetsa chimphepo chamkuntho.—Maliko 4:36-41.
adzakonza zinthu zonse zimene zawonongedwa padzikoli.—Yesaya 35:1, 2.
anadyetsa anthu ambiri modabwitsa.—Mateyu 14:17-21.
adzathetsa njala padziko lonse.—Salimo 72:16.
anachiritsa anthu ambiri.—Luka 18:35-43.
adzathetsa matenda onse.—Yesaya 33:24.
anaukitsa anthu amene anamwalira.—Luka 8:49-55.
adzathetsa imfa.—Chivumbulutso 21:3, 4.
6. Madalitso amene Ufumu wa Mulungu udzabweretse
Ufumu wa Mulungu udzachititsa kuti anthu azikhala moyo wabwino ngati mmene Yehova ankafunira poyamba. Anthu adzakhala ndi moyo m’paradaiso padzikoli mpaka kalekale. Onerani VIDIYO kuti muone mmene Yehova akukwaniritsira cholinga chake pogwiritsa ntchito Mwana wake Yesu.
Werengani Salimo 145:16, kenako mukambirane funso ili:
Kodi mumamva bwanji mukaganizira kuti Yehova ‘adzakhutiritsa zokhumba za chamoyo chilichonse’?
ZIMENE ENA AMANENA: “Ngati titamachita zinthu mogwirizana, tikhoza kuthetsa mavuto apadziko lonse.”
Kodi Ufumu wa Mulungu udzathetsa mavuto ati amene maboma a anthu alephera kuwathetsa?
ZOMWE TAPHUNZIRA
Ufumu wa Mulungu udzakwaniritsa cholinga chimene Mulungu anali nacho poyamba. Udzachititsa dzikoli kuti likhale paradaiso, momwe mudzakhale anthu abwino omwe azidzalambira Yehova mpaka kalekale.
Kubwereza
Kodi Ufumu wa Mulungu udzachititsa bwanji kuti dzina la Yehova liyeretsedwe?
N’chifukwa chiyani timakhulupirira kuti Ufumu wa Mulungu udzakwaniritsa zonse zimene Baibulo linalonjeza?
Pa madalitso onse amene Ufumu wa Mulungu udzabweretse, ndi dalitso liti limene inuyo mukuliyembekezera kwambiri?
ONANI ZINANSO
Fufuzani kuti mudziwe zimene nkhondo ya Aramagedo imatanthauza.
“Kodi Nkhondo ya Aramagedo Idzakhala Yotani?” (Nkhani yapawebusaiti)
Werengani nkhaniyi kuti mudziwe zomwe zidzachitike pa nthawi imene Yesu anaitchula kuti “chisautso chachikulu.”—Mateyu 24:21.
“Kodi Chisautso Chachikulu N’chiyani?” (Nkhani yapawebusaiti)
Onani zimene zingathandize mabanja kuyerekezera kuti ali m’Paradaiso.
Munkhani yakuti, “Ndinali Ndi Mafunso Ambiri Omwe Ankandisowetsa Mtendere,” onani zimene zinathandiza munthu wina woukira boma kupeza mayankho a mafunso omwe ankamusowetsa mtendere.
“Baibulo Limasintha Anthu” (Nsanja ya Olonda, January 1, 2012)
-