-
Yehova Mulungu Wathu Ali WachifundoNsanja ya Olonda—1989 | March 1
-
-
Bwererani kwa Yehova
Ngakhale awo amene amalakwa mokulira angabwerere kwa Yehova ndi kusonyezedwa chifundo. (Salmo 145:8, 9) Hoseya kachiŵirinso analozera ku chisamaliro chachifundo cha Mulungu kwa Aisrayeli. Ngakhale kuti mtunduwo unatembenuka motsutsana ndi Yehova, iye analonjeza kubwezeretsedwanso, akumanena kuti: ‘Ndidzawawombola ku mphamvu ya [Sheol, NW]; ndidzawawombola kuimfa.’ Samariya (Israyeli) anakayenera kulipira mtengo kaamba ka kuwukira. Koma Aisrayeli anafulumizidwa kubwerera kwa Mulungu ndi mawu owona mtima, ‘milomo ya ng’ombe zazing’ono.’ Ulosiwo unamaliza ndi lingaliro lotonthoza lakuti anzeru ndi olunjika omwe amayenda m’njira zowongoka za Yehova adzasangalala ndi chifundo chake ndi chikondi.—13:1–14:9.
-
-
Yehova Mulungu Wathu Ali WachifundoNsanja ya Olonda—1989 | March 1
-
-
○ 13:14—Yehova sakanalekerera Aisrayeli osamverawo mwa kuwapulumutsa iwo pa nthaŵi imeneyo kuchoka ku mphamvu ya Sheol kapena kuwalanditsa iwo ku imfa. Iye sakasonyeza kumvera chifundo, popeza kuti iwo sanayenerere chifundo. Koma mtumwi Paulo anasonyeza kuti Mulungu potsirizira pake akameza imfa kotheratu ndi kuthetsa chilakiko chake. Yehova anasonyeza mphamvu yake ya kuchita tero mwa kuwukitsa Yesu Kristu kuchokera ku imfa ndi Sheol, mwakutero kupereka chitsimikiziro chakuti anthu m’chikumbukiro cha Mulungu adzawukitsidwa ndi Mwana wake pansi pa ulamuliro wa Ufumu.—Yohane 5:28, 29.
-