-
Anaphunzira pa Zolakwa ZakeTsanzirani Chikhulupiriro Chawo
-
-
12. (a) N’chifukwa chiyani sitiyenera kuganiza kuti Yona anagona chifukwa chakuti analibe nazo ntchito zimene zinkachitikazo? (Onaninso mawu a m’munsi.) (b) Kodi Yehova anathandiza bwanji anthuwo kudziwa chimene chinayambitsa vuto?
12 Chifukwa chothedwa nzeru, Yona anapita m’chipinda cha pansi pa sitimayo n’kugona tulo tofa nato.b Mkulu wa oyendetsa sitima atam’peza, anamudzutsa n’kumuuza kuti nayenso apemphere kwa mulungu wake. Poona kuti chimphepochi chinali chachilendo, anthuwo anachita maere kuti adziwe munthu amene wawabweretsera tsoka limeneli. N’zachidziwikire kuti mtima wa Yona unagunda kwambiri ataona kuti maerewo sakugwera aliyense mwa anthuwo. Posakhalitsa Yona anadziwa kuti Yehova ndi amene ankachititsa chimphepocho ndi kutsogolera maerewo n’cholinga choti aliyense adziwe kuti wolakwa sanali wina ayi koma Yonayo.—Werengani Yona 1:5-7.
-
-
Anaphunzira pa Zolakwa ZakeTsanzirani Chikhulupiriro Chawo
-
-
b Baibulo la Septuagint limanena kuti Yona anagona tulo mpaka kufika poliza nkonono. Komabe tisaganize kuti Yona anagona chifukwa choti analibe nazo ntchito zimene zinkachitikazo. Tisaiwale kuti anthu ena amagona kwambiri akakhala ndi nkhawa. Mwachitsanzo, pamene zinthu zinavuta kwambiri m’munda wa Getsemane, Yesu atatsala pang’ono kugwidwa, Petulo, Yakobo, ndi Yohane ‘anagona chifukwa cha chisoni.’—Luka 22:45.
-