-
Muzikhulupirira Yehova Kuti Mukhale ndi MoyoNsanja ya Olonda (Yophunzira)—2018 | November
-
-
7. Kodi Yehova anatani atamva madandaulo a Habakuku?
7 Werengani Habakuku 1:5-7. Habakuku atafotokozera Yehova nkhawa zake, ayenera kuti ankayembekezera kuti aone mmene Yehova angamuyankhire. Popeza Yehova ndi wachifundo komanso womvetsa zinthu, sanakalipire Habakuku chifukwa chomudandaulira. Iye ankadziwa kuti mneneri wakeyo wachita zimenezo chifukwa chopanikizika ndi mavuto. Choncho anamuuza mawu opita kwa Ayuda osamvera ofotokoza zimene zichitike pasanapite nthawi yaitali. N’kutheka kuti Habakuku anali woyamba kuuzidwa ndi Yehova kuti mapeto a zinthu zoipazo ali pafupi kwambiri.
8. N’chifukwa chiyani Habakuku anadabwa ndi yankho la Yehova?
8 Yehova anasonyeza Habakuku kuti anali wokonzeka kuthetsa zoipazo. Anali atangotsala pang’ono kulanga anthu oipa komanso ankhanzawo. Ponena kuti “m’masiku anu” Yehova ankatanthauza kuti apereka chiweruzocho Habakukuyo kapena Aisiraeli anzake a pa nthawiyo ali moyo. Zimene Yehova ananenazi si zimene Habakuku ankayembekezera. Kodi zimenezi zinayankha mafunso ake odandaula aja? Mawu amene Yehova anamuuza anasonyeza kuti Ayuda adzavutika kwambiri.a Akasidi (Ababulo) anali oipa mtima komanso ankhanza kuposa anthu amtundu wa Habakuku omwe ankadziwa mfundo za Yehova. Nanga n’chifukwa chiyani Yehova anasankha kugwiritsa ntchito mtundu wosalambira Mulungu komanso wankhanzawu kuti ulange anthu ake? Kodi mukanakhala kuti ndi inuyo amene mukuuzidwa zimenezi, mukanatani?
-
-
Muzikhulupirira Yehova Kuti Mukhale ndi MoyoNsanja ya Olonda (Yophunzira)—2018 | November
-
-
a Lemba la Habakuku 1:5 limati “anthu inu” posonyeza kuti tsoka limene linkabweralo linadzakhudza dziko lonse la Yuda.
-