Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Kusangalala mwa Mulungu wa Chipulumutso Chathu
    Nsanja ya Olonda—2000 | February 1
    • 14-16. Malinga ndi Habakuku 3:14, 15, kodi n’chiyani chomwe chidzachitikire anthu a Yehova komanso adani awo?

      14 Pa Armagedo, awo amene akuyesa kuwononga “odzozedwa” a Yehova adzasokonezedwa maganizo. Malinga ndi Habakuku 3:14, 15, mneneriyu akulankhula ndi Mulungu kuti: “Munapyoza ndi maluti ake mutu wa ankhondo ake; anadza ngati kavumvulu kundimwaza; kukondwerera kwawo kunanga kufuna kutha ozunzika mobisika. Munaponda panyanja ndi akavalo anu, madzi amphamvu anaunjikana mulu.”

  • Kusangalala mwa Mulungu wa Chipulumutso Chathu
    Nsanja ya Olonda—2000 | February 1
    • 16 Komanso pali zambiri zomwe zidzachitika. Yehova adzagwiritsa ntchito magulu auzimu, amphamvu zoposa za anthu kumalizitsa kuwononga adani akewo. Ndi “akavalo” a ankhondo ake a kumwamba otsogozedwa ndi Yesu Kristu, iye adzapitabe patsogolo mwachipambano kudutsa “panyanja” ndi ‘pamadzi amphamvu ounjikana mulu,’ ndiko kuti, chiŵerengero chomawonjezereka cha anthu achidani. (Chivumbulutso 19:11-21) Ndiyeno oipa adzachotsedwa padziko lapansi. Mphamvu za Mulungu ndi chilungamo chake zidzasonyezedwatu mwamphamvu kwambiri!

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena