Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Masiku Otsiriza—Nthaŵi ya Kututa
    Nsanja ya Olonda—1988 | January 1
    • 9. Ndani amene ali achatsopano amenewo, ndipo kodi ndi maulosi ena ati amene amatchula kuwonekera kwawo mkati mwa “masiku otsiriza”?

      9 Achatsopano amenewa amayang’ana kutsogolo ku kusangalala ndi moyo m’Paradaiso padziko lapansi pansi pa Mfumu yoikidwa ya Yehova. (Masalmo 37:11, 29; 72:7-9) Kusonkhanitsidwa kwawo kunanenedweratu mu unyinji wa maulosi ena. Yesaya, mwachitsanzo, ananeneratu kuti “m’masiku otsiriza” mitundu idzanka kunyumba ya Yehova. (Yesaya 2:2, 3) Hagai analosera kugwedezeka kwa mitundu mkati mwa kumene “zofunika za amitundu onse zidzafika.” (Hagai 2:7) Zekariya analankhula za “amuna khumi a manenedwe onse amitundu” omwe adzazigwirizanitsa iwo eni kwa anthu a Mulungu. (Zekariya 8:23) Kuwonjezerapo, Yesu iyemwini analosera ponena za “khamu lalikulu” limeneli. Iye ananena kuti: “Koma pamene Mwana wa munthu adzadza mu ulemerero wake, ndi angelo onse pamodzi naye, pomwepo iye adzakhala pa chimpando cha kuwala kwake. Ndipo adzasonkhanidwa pamaso pake anthu a mitundu yonse, ndipo iye adzalekanitsa iwo wina ndi mnzake, monga mbusa alekanitsa nkhosa ndi mbuzi. Nadzakhalitsa nkhosa ku dzanja lake lamanja, koma mbuzi kulamanzere.”​—Mateyu 25:31-33.

  • Masiku Otsiriza—Nthaŵi ya Kututa
    Nsanja ya Olonda—1988 | January 1
    • 14. Ndi anthu a mtundu wanji amene akusonkhanitsidwa mu gulu la Yehova?

      14 Ndithudi, anthu a Mulungu sali okondweretsedwa m’chiwonjezeko kokha chifukwa cha icho chokha. Iwo amadziŵa, ngakhale kuli tero, kuti onse a awo achatsopano obwera ku gulu la Yehova ali “zinthu zofunika” m’maso mwa Yehova. Ambiri anali “kulira ndi kuusa moyo pa zonyansa zonse” zimene anachitira umboni m’Chikristu cha Dziko. (Ezekieli 9:4) Iwo akunka ku “phiri la Yehova” chifukwa akufuna kulangizidwa m’njira za Mulungu. (Yesaya 2:2, 3) Ndi chitsimikiziro champhamvu chotani nanga cha dalitso la Yehova​—kuti m’dongosolo iri la kachitidwe ka zinthu loipa ndi lokondetsa zinthu za kuthupi, mazana a zikwi za atsopano amadziwonetsera iwo eni chaka chirichonse monga “zinthu zofunika” za Yehova!

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena