-
Nthawi ya Kuyesedwa ndi KusefedwaNsanja ya Olonda—1987
-
-
Nthawi ya Kuyesedwa ndi Kusefedwa
“Ndipo Ambuye yemwe mumfuna adzadza ku kachisi wake modzidzimutsa; [ndiponso ndi NW] mthenga wa chipangano . . . ndipo adzakhala ndi kuyenga ndi kuyeretsa.”—MALAKI 3:1, 3.
-
-
Nthawi ya Kuyesedwa ndi KusefedwaNsanja ya Olonda—1987
-
-
3. Kodi nchiyani chimene chinaphatikizidwamo mu ntchito ya kuyenga ya makedzana?
3 Koma, choyamba, kodi nchifukwa ninji Yehova amaika anthu ake pa kuyesedwa ndi kusefedwa? Monga “wosanthula mitima,” iye anakonzekera kuyenga anthu ake olinganizidwa. (Miyambo 17:3; Masalmo 66:10) Mu nthawi za Baibulo ntchito ya kuyenga inaphatikizapo kutentha chitsulo ku mlingo wakusungunuka ndipo kenaka kuchotsa zoipa kapena mphala. Timawerenga: “Woyenga amayang’ana kachitidweko, kaya ataimilira kapena kukhala pansi, ndi kuyang’anitsitsa kosamalitsa, kufikira. . . chitsulo [chamadzi] chikhala ndi kawonekedwe ka kalilole wopukutidwa bwino, kuunikira chinthu chirichonse chozungulira icho; ngakhale woyenga, pamene akuyang’ana pa chitsulo, angadziwone iye mwini ngati kuti akuyang’ana pa kalilole, ndipo chotero iye angapange chiweruzo cholondola kwambiri ponena za kuyera kwa chitsulocho. Ngati iye wakhutiritsidwa, moto umachotsedwa, ndipo chitsulo chimachotsedwa m’ng’anjo; koma ngati sichinalingaliridwe kukhala choyera, ntovu wowonjezereka umaikidwa ndipo ntchitoyo imabwerezedwa.”(Cyclopedia of Biblical, Theological, and Ecclesiastical Literature, yolembedwa ndi J. McClintock ndi J. Strong) Golide kapena siliva woyengedwa motero anali wamtengo wapatali.—Yerekezani ndi Chivumbulutso 3:18.
4. Kodi nchifukwa ninji Yehova walola kuyesedwa ndi kusefedwa pakati pa anthu ake?
4 Yehova amalola kuyesedwa ndi kusefedwa kotero kuti ayenge, kapena kuyeretsa, anthu ake, kuwathandiza iwo kuunikira molongosoka chifaniziro chake. (Aefeso 5:1) Muntchito ya kuyenga, iye amachotsa mphala mwa kuyeretsa ziphunzitso zonyansa ndi machitachita. (Yesaya 1:25) Iye amasefanso kuchokera pakati pa anthu ake awo amene amakana kugonjera ku ntchito yoyenga ndi iwo amene “amakhala chokhumudwitsa ndi anthu amene amachita kusayeruzika.” Ichi chimayeretsa njira kaamba ka “ana a ufumu,” Israyeli wauzimu, kuti awale ndi kunyezimira kotero kuti gulu la padziko lapansi lingasonkhanitsidwe ndi kumamatira kwa iwo mwa gulu kaamba ka kupulumuka.—Mateyu 13:38, 41, 43; Afilipi 2:15.
-