-
Yehova Amawerenga ‘Tsitsi Lonse la M’mutu Mwanu’Nsanja ya Olonda—2005 | August 1
-
-
6 Pofuna kuthandiza atumwi ake kumvetsetsa chifukwa chimene sayenera kuchitira mantha, Yesu anapereka mafanizo awiri. Iye anawauza kuti: ‘Kodi mpheta ziwiri sizigulidwa kakobiri? Ndipo imodzi ya izo siigwa pansi popanda Atate wanu [kudziwa]: komatu inu, tsitsi lonse la m’mutu mwanu amaliwerenga. Chifukwa chake musamawopa; inu mupambana mpheta zambiri.’ (Mateyu 10:29-31) Onani kuti malingana ndi mawu a Yesuwa, kuti tisachite mantha pa mavuto m’pofunika kuti tisamakayikire kuti Yehova amatiganizira ifeyo patokha. Zikuoneka kuti mtumwi Paulo sankakayikira mfundo imeneyi. Iye analemba kuti: “Ngati Mulungu ali ndi ife, adzatikaniza ndani? Iye amene sanatimana Mwana wake wa iye yekha, koma anam’pereka chifukwa cha ife tonse, adzalekeranji kutipatsanso ife zinthu zonse kwaulere pamodzi ndi iye?” (Aroma 8:31, 32) Ngakhale mutakumana ndi mavuto aakulu motani, inunso panokha musamakayikire ngakhale pang’ono kuti Yehova amakuganizirani panthawi yonse imene muli wokhulupirika kwa iye. Poona mwatsatanetsatane mawu amene Yesu ananena polimbikitsa atumwi ake, titsimikizira mfundo imeneyi.
-
-
Yehova Amawerenga ‘Tsitsi Lonse la M’mutu Mwanu’Nsanja ya Olonda—2005 | August 1
-
-
10. Kodi mawu akuti ‘tsitsi lonse la m’mutu mwanu amaliwerenga’ amasonyeza mfundo yofunika yotani?
10 Kuphatikiza pa chitsanzo cha mpheta, Yesu anati: ‘Tsitsi lonse la m’mutu mwanu amaliwerenga.’ (Mateyu 10:30) Mawu achidule koma ozamawa amagogomezera kwambiri mfundo imene ili m’chitsanzo cha Yesu chija chonena za mpheta. Taganizirani izi: Anthu ambiri amakhala ndi tsitsi pafupifupi 100,000 m’mutu mwawo. Katsitsi kalikonse pakokha sikasiyana ndi tsitsi lina lonselo ndipo palibe katsitsi kalikonse kamene timachita kukaganizira pakokha. Komatu katsitsi kalikonse Yehova Mulungu amakaona ndiponso amakawerenga. Motero kodi pali chinthu chilichonse chokhudza moyo wathu chimene Yehova sangadziwe? Ndithu, Yehova amamvetsa mmene mtumwi wake aliyense payekhapayekha alili. Inde, iye amathadi ‘kuyang’ana mumtima.’—1 Samueli 16:7.
11. Kodi Davide anasonyeza bwanji kuti sankakayikira ngakhale pang’ono kuti Yehova amamuganizira iyeyo payekha?
11 Davide, yemwe ankadziwa bwino mavuto, sankakayika kuti Yehova amamuganizira. Davideyo analemba kuti: “Munandisanthula, Yehova, nimundidziwa. Inu mudziwa kukhala kwanga ndi kuuka kwanga, muzindikira lingaliro langa muli kutali.” (Salmo 139:1, 2) Inunso musakayikire n’komwe kuti Yehova amakudziwani bwino. (Yeremiya 17:10) Musamafulumire kuganiza kuti Yehova sakuwerengerani inuyo panokha, podziona kuti ndinu wosafunika kwenikweni, chifukwatu n’zosatheka kuti inuyo mulephere kuonedwa ndi maso a Yehova oona zinthu zonse.
-