-
Kodi Khoka ndi Nsomba Zimatanthauzanji kwa Inu?Nsanja ya Olonda—1992 | June 15
-
-
3. Kodi kumvetsa mafanizo a Yesu kungatipindulitse motani?
3 Ndiyeno Yesu anagwiritsira ntchito Yesaya 6:9, 10, amene anafotokoza za anthu amene adali ogontha ndi akhungu mwauzimu. Komabe, ife sitiyenera kukhala otero. Ngati timvetsetsa ndi kuchitapo kanthu pamafanizo ake, tingakhale achimwemwe kwambiri—tsopano ndi mtsogolo mosatha. Yesu akutitsimikizira mwaubwenzi kuti: “Maso anu ali odala, chifukwa apenya; ndi makutu anu chifukwa amva.” (Mateyu 13:16) Chitsimikiziro chimenecho chikuphatikizapo mafanizo onse a Yesu, komano tiyeni tisumike maganizo pafanizo lalifupi la khoka, lolembedwa pa Mateyu 13:47-50.
Fanizo Lokhala ndi Tanthauzo Lozama
4. Kodi Yesu anasimbanji mwafanizo, monga momwe kwalembedwera pa Mateyu 13:47-50?
4 “Ndiponso, ufumu wa kumwamba uli wofanana ndi khoka loponyedwa m’nyanja, ndi kusonkhanitsa pamodzi za mitundu yonse; limene podzala, analivuulira pamtunda; ndipo m’mene anakhala pansi, anazisonkhanitsa zabwino m’zotengera, koma zoipa anazitaya kuthengo. Padzatero pa chimaliziro cha nthaŵi ya pansi pano: angelo adzatuluka, nadzawasankhula oipa pakati pa abwino, nadzawataya m’ng’anjo yamoto; komweko kudzakhala kulira ndi kukukuta mano.”
-
-
Kodi Khoka ndi Nsomba Zimatanthauzanji kwa Inu?Nsanja ya Olonda—1992 | June 15
-
-
7. Kodi Yesu anali kuchitira fanizo chiyani pamene analankhula za nsomba?
7 Mogwirizana ndi zimenezo, nsomba za m’fanizo lino zimaimira anthu. Chifukwa chake, pamene vesi 49 limalankhula za kulekanitsa oipa kwa olungama, limasonya, osati kwa zolengedwa za m’nyanja zolungama kapena zoipa, koma anthu olungama kapena oipa. Mofananamo, vesi 50 siliyenera kutipangitsa kulingalira za nyama za m’nyanja zimene zimalira kapena kukukuta mano awo. Ayi. Fanizoli likunena za kusonkhanitsidwa kwa anthu ndi kulekanitsidwa kwawo kotsatirapo, kumene kuli nkhani yaikulu kwambiri, monga momwe zotulukapo zake zimasonyezera.
8. (a) Kodi tingaphunzire chiyani pachotulukapo cha nsomba zosayenera? (b) Polingalira za zimene zinanenedwa ponena za nsomba zosayenera, kodi tingatsimikizirenji ponena za Ufumu?
8 Onani kuti nsomba zosayenera, ndiko kuti oipa, adzaponyedwa m’ng’anjo yamoto, kumene kudzakhala kulira ndi kukukuta mano. Kwinakwake, Yesu anagwirizanitsa kulira koteroko ndi kukukuta mano kukhala kunja kwa Ufumu. (Mateyu 8:12; 13:41, 42) Pa Mateyu 5:22 ndi 18:9, anatchuladi ‘Gehena wamoto,’ kusonyeza chiwonongeko chosatha. Kodi zimenezo sizimasonyeza mmene kuliri kofunika kupeza tanthauzo la fanizo limeneli ndi kuchitapo kanthu moyenera? Tonsefe tidziŵa kuti mu Ufumu wa Mulungu mulibe kapena simudzakhala oipa. Chifukwa chake, pamene Yesu ananena kuti “ufumu wa kumwamba uli wofanana ndi khoka,” ayenera kukhala anatanthauza kuti mogwirizana ndi Ufumu wa Mulungu, muli mbali yofanana ndi khoka loponyedwa kuti ligwire nsomba za mitundumitundu.
-