Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • mwb18 February tsamba 8
  • Tizipewa Kuchita Zinthu Zimene Zingakhumudwitse Ena

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • Tizipewa Kuchita Zinthu Zimene Zingakhumudwitse Ena
  • Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2018
  • Nkhani Yofanana
  • Anthu Okonda Yehova ‘Alibe Chowakhumudwitsa’
    Nsanja ya Olonda—2013
  • “Chirimikani”—Musakhumudwe
    Nsanja ya Olonda​—1990
  • Kodi Mudzakhumudwa N’kusiya Kutsatira Yesu?
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2021
  • Okonda Chilungamo Palibe Chowakhumudwitsa
    Nsanja ya Olonda Yolengeza Ufumu wa Yehova (Yophunzira)—2021
Onani Zambiri
Utumiki Komanso Moyo Wathu wa Chikhristu—Ndandanda ya Misonkhano—2018
mwb18 February tsamba 8

CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU | MATEYU 18-19

Tizipewa Kuchita Zinthu Zimene Zingakhumudwitse Ena

Yesu anagwiritsa ntchito mafanizo pophunzitsa anthu za kuopsa kochita zinthu zimene zingatipunthwitse komanso kukhumudwitsa ena.

18:6, 7

  • Mawu akuti “zopunthwitsa” akutanthauza zochita kapena zinthu zina zimene zingachititse munthu kuti achite zinthu zolakwika, kapenanso achite tchimo

  • Munthu wokhumudwitsa ena zikanakhala bwino kumuponya m’nyanja atamangiriridwa chimwala cha mphero m’khosi mwake

Mwala wamphero ukukokedwa ndi bulu; mwala wamphero womangiriridwa pakhosi la munthu yemwe akuponyedwa m’nyanja

Mwala wa mphero

18:8, 9

  • Yesu anauza otsatira ake kuti ayenera kuchotsa ngakhale chiwalo chawo chofunika kwambiri monga dzanja kapena diso ngati akuona kuti chiwalocho chikuwachititsa kuti achite tchimo

  • Kuli bwino kukhala wopanda chinthu chinachake chimene timachikonda kwambiri n’kudzalowa mu Ufumu wa Mulungu kusiyana ndi kukhala ndi chinthucho koma n’kudzaponyedwa m’Gehena, yemwe akutanthauza kuwonongedwa kotheratu

Kodi n’chiyani pa moyo wanga chimene chingakhale chopunthwitsa, nanga ndingatani kuti ndizipewa zinthu zimene zingandipunthwitse komanso kukhumudwitsa ena?

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena