-
Mungabweze Mbale WanuNsanja ya Olonda—1999 | October 15
-
-
Kupeza Chithandizo Chokhwima
12, 13. (a) Yesu analongosola mbali yachiŵiri iti yothetsera milandu? (b) Kodi pali malangizo oyenerera otani pochita mbali imeneyi?
12 Kodi inuyo mungakonde kuti ena angokulekererani mwamsanga mutapanga cholakwa chachikulu? Kutalitali. Ndiye chifukwa chake Yesu anasonyeza kuti mutachita mbali yoyamba, simuyenera kuleka kuyesa kubweza mbale wanu, kuti akhalebe wogwirizana nanu ndi ena polambira Mulungu m’njira yovomerezeka. Yesu anafotokoza mbali yachiŵiri: “Ngati samvera, onjeza kutenga ndi iwe wina mmodzi kapena aŵiri, kuti atsimikizidwe mawu onse pakamwa pa mboni ziŵiri kapena zitatu.”
13 Iye ananena kuti mutenge “wina mmodzi kapena aŵiri.” Sananene kuti mutachita mbali yoyamba, muli ndi ufulu wokambirana nkhani imeneyo ndi ena ambiri, kuonana ndi woyang’anira woyendayenda, kapena kulembera abale ena za vuto limenelo. Kaya mukhale wotsimikiza mtima chotani za cholakwacho, mulibe umboni wonse wofunikira. Simuyenera kufalitsa nkhani zoipa zimene zidzakupangitsani kukhala kazitape. (Miyambo 16:28; 18:8) Koma Yesu anati muyenera kutenga munthu winanso mmodzi kapena enanso aŵiri. Chifukwa chiyani? Nanga amenewo angakhale anthu otani?
14. Kodi tingatenge anthu ati pokakamba naye kachiŵiri?
14 Mukuyesa kubweza mbale wanu mwa kum’tsimikizira kuti wachita tchimo ndipo mwa kum’limbikitsa kulapa kuti akhale pamtendere ndi inu ndiponso ndi Mulungu. Kuti muchite zimenezo, zingakhale bwino kwambiri ngati “mmodzi kapena aŵiri” amenewo ali mboni za cholakwacho. Mwina analipo pamene iye anachimwa, kapena mwina ali ndi mfundo zenizeni zokhudza chimene chinachitikacho (kapena chimene sichinachitidwe) m’nkhani yabizinesi. Ngati mboni zoterozo palibe, awo amene mukutenga angakhale anthu odziŵa nkhani zimenezo ndipo angathe kudziŵa ngati zimene zinachitika zinalidi zolakwika. Komanso, ngati zingafunikire pambuyo pake, angakhale mboni ya zimene zinanenedwa, kutsimikizira mfundo zoperekedwazo ndi kuyesayesa komwe kunapangidwa. (Numeri 35:30; Deuteronomo 17:6) Chotero si anthu oti sanena chilichonse, kapena oweruza; koma amakhalapo kuti athandize kubweza mbale wanu ndi wawo.
15. N’chifukwa chiyani akulu achikristu angakhale othandiza pamene tikuchita mbali yachiŵiri?
15 Musaganize kuti awo amene mudzatenga afunikira kukhala akulu a mumpingo. Komabe, amuna okhwima amene ali akulu angathandizire chifukwa cha ziyeneretso zawo zauzimu. Akulu amenewo ali “monga pobisalira mphepo, ndi pousira chimphepo; monga mitsinje yamadzi m’malo ouma, monga mthunzi wa thanthwe lalikulu m’dziko lotopetsa.” (Yesaya 32:1, 2) Amadziŵa kukambirana ndi abale ndi alongo ndi kuwawongolera. Ndipo wolakwayo ali ndi chifukwa chabwino chosonyezera chidaliro mwa “mphatso za amuna” zimenezi.c (Aefeso 4:8, 11, 12, NW) Kukamba nkhani imeneyi pamaso pa anthu okhwima oterowo ndi kupemphera nawo kungasinthe mkhalidwe wonse ndi kuthetsa nkhani yomwe inkaoneka ngati yosatheka.—Yerekezani ndi Yakobo 5:14, 15.
-
-
Mungabweze Mbale WanuNsanja ya Olonda—1999 | October 15
-
-
c Katswiri wina wodziŵa Baibulo anati: “Nthaŵi zina zimachitika kuti wolakwa amamvetsera kwambiri aŵiri kapena atatu enawo (makamaka ngati ndi anthu olemekezeka) kusiyana ndi munthu mmodzi, makamaka ngati munthuyo ndi amene wasiyana naye maganizo.”
-