-
Antchito m’Munda WampesaNsanja ya Olonda—1989 | August 15
-
-
Pomalizira, tsiku logwira ntchito lophiphiritsiralo likutha ndi imfa ya Yesu, ndipo nthaŵi ikubwera ya kulipira antchitowa. Lamulo la nthaŵi zonse lolipirira womalizira ndi woyamba likutsatiridwa, monga momwe likulongosoledwera: “Ndipo pamadzulo, mwini munda anati kwa kapitawo wake, kaitane antchito nuwapatse iwo kulipira kwawo, uyambe kwa omalizira kufikira kwa woyamba. Ndipo pamene iwo olembedwa poyandikira madzulo anadza, analandira munthu aliyense rupiya latheka limodzi. Ndipo mmene oyamba anadza, analingalira kuti adzalandira kopambana, ndipo iwonso analandira onse rupiya latheka. Koma mmene iwo analandira, anaderera kwa mwini banja, nati, Omalizira awa anagwira ntchito mphindi yaing’ono ndipo munawalinganiza ndi ife amene tinapirira kuwawa kwa dzuŵa ndi kutentha kwake. Koma iye anayankha, nati kwa mmodzi wa iwo, Mnzanga, sindikunyenga iwe; kodi iwe sunapangana ndi ine pa rupiya latheka limodzi? Tenga lako, numuke; pakuti ine ndifuna kupatsa kwa uyu womalizira monga kwa iwe. Sikuloleka kodi kwa ine kuchita chimene ndifuna ndi zanga? Kapena diso lako laipa kodi chifukwa ine ndiri wabwino?” M’kumaliza Yesu anabwereza nsonga yopangidwa poyambirirapo, akumanena kuti: “Omalizira adzakhala oyamba, ndipo oyamba adzakhala omalizira.”
-
-
Antchito m’Munda WampesaNsanja ya Olonda—1989 | August 15
-
-
Mwamsanga awo olembedwa ntchito poyamba anawona kuti ophunzira a Yesu analipiridwa, ndipo iwo anawona iwo akugwiritsira ntchito rupiya lawo latheka lophiphiritsira. Koma iwo anafuna zoposa mzimu woyera ndi mwaŵi wake wa Ufumu woyanjana nawo. Kung’ung’udza kwawo ndi zitsutso zinatenga mtundu wa kuzunza ophunzira a Kristu, antchito m’munda wampesa “otuluka madzulo.”
Kodi kukwaniritsidwa kwa m’zana loyamba kumeneku kuli kukwaniritsidwa kokha kwa fanizo la Yesu? Ayi, atsogoleri achipembedzo a Chikristu cha Dziko m’zana la 20 lino, chifukwa cha malo awo ndi mathayo, akhala “oyamba” kulembedwa ntchito m’munda wampesa wophiphiritsira wa Mulungu. Iwo analingalira olalikira odzipereka oyanjana ndi Watch Tower Bible and Tract Society kukhala “omalizira” kukhala ndi thayo lirilonse lotsimikizirika mu utumiki wa Mulungu. Koma, m’chenicheni, ali amenewa amene atsogoleri achipembedzo ananyoza omwe alandira rupiya latheka—ulemu wa kutumikira monga oimira odzozedwa a Ufumu wakumwamba wa Mulungu. Mateyu 19:30–20:16.
-