-
Kodi Chimwemwe Chenicheni Chingapezeke Kuti?Nsanja ya Olonda—1997 | March 15
-
-
Pa Ulaliki wake wa pa Phiri, Yesu Kristu anati: “Achimwemwe ali awo ozindikira kusoŵa kwawo kwauzimu, popeza kuti ufumu wakumwamba uli wawo.” (Mateyu 5:3, NW) Yesu anatinso: “Mudzisungire kupeŵa msiriro uliwonse; chifukwa moyo wake wa munthu sulingana ndi kuchuluka kwa zinthu zake ali nazo.”—Luka 12:15.
-
-
Kodi Chimwemwe Chenicheni Chingapezeke Kuti?Nsanja ya Olonda—1997 | March 15
-
-
Pofunafuna chimwemwe ena amayesa kusumika maganizo pa umunthu wawo mwa kuyesa kudzikulitsira ulemu wa iwo okha. Malaibulale ndi masitolo a mabuku ngodzaza ndi mabuku odziphunzitsa munthu yekha, koma zofalitsa zimenezi sizinapatse anthu chimwemwe chokhalitsa. Choncho, kodi nkuti kumene tingapeze chimwemwe chenicheni?
Kuti tikhaledi achimwemwe, tiyenera kudziŵa kusoŵa kwathu kwauzimu kwachibadwa. Yesu anati: “Achimwemwe ali awo ozindikira kusoŵa kwawo kwauzimu.” Komanso, sitingapeze phindu lililonse ngati tadziŵa kusoŵa kumeneku kenako nkulephera kuchitapo kanthu. Tinene mwafanizo: Nchiyani chingachitikire wampikisano wothamanga yemwe walephera kukhutiritsa chikhumbo cha madzi cha thupi lake pambuyo pa mpikisanowo? Kodi mwamsanga sangathedwe madzi m’thupi ndi kudwala matenda ena aakulu? Momwemonso, ngati tilephera kukhutiritsa njala yathu ya chakudya chabwino chauzimu, tidzafota mwauzimu m’kupita kwa nthaŵi. Zimenezi zidzatitayitsa chisangalalo ndi chimwemwe.
-