-
Chilamulo cha Pakamwa—Kodi N’chifukwa Chiyani Chinalembedwa?Nsanja ya Olonda—1999 | January 15
-
-
KODI n’chifukwa chiyani Ayuda ambiri a m’zaka za zana loyamba sanalandire Yesu monga Mesiya? Mboni ina yoona ndi maso inati: “Mmene iye [Yesu] analoŵa m’Kachisi, ansembe aakulu ndi akulu a anthu anadza kwa iye analikuphunzitsa, nanena, Muchita izi ndi ulamuliro wotani? Ndipo ndani anakupatsani ulamuliro wotere?” (Mateyu 21:23) Kwa iwo, Wamphamvuyonse anapatsa mtundu wachiyuda Torah (Chilamulo), ndipo iyo inapatsa anthu ena ulamuliro wochokera kwa Mulungu. Kodi Yesu anali ndi ulamuliro umenewo?
Yesu anasonyeza ulemu waukulu pa Torah ndi kwa awo amene inawapatsadi ulamuliro. (Mateyu 5:17-20; Luka 5:14; 17:14) Koma nthaŵi zambiri anadzudzula anthu amene anadumpha malamulo a Mulungu. (Mateyu 15:3-9; 23:2-28) Anthu amenewa anali kutsatira miyambo imene inadzadziŵika kuti chilamulo cha pakamwa. Yesu anachikana. Chotero, ambiri anam’kana kuti si Mesiya. Iwo ankakhulupirira kuti munthu amene amachirikiza miyambo ya awo amene anali ndi ulamuliro pakati pawo ndi yekhayo amene angakhale ndi Mulungu.
-
-
Chilamulo cha Pakamwa—Kodi N’chifukwa Chiyani Chinalembedwa?Nsanja ya Olonda—1999 | January 15
-
-
“Ndani Anakupatsani Ulamuliro Wotere?”
N’zosakayikitsa kuti Chilamulo cha Mose chinasiyira ansembe, mbadwa za Aroni, ulamuliro waukulu pa zachipembedzo ndi kulangiza. (Levitiko 10:8-11; Deuteronomo 24:8; 2 Mbiri 26:16-20; Malaki 2:7) Koma m’kupita kwa zaka mazana ambiri, ansembe ena anakhala osakhulupirika nakhalanso achinyengo. (1 Samueli 2:12-17, 22-29; Yeremiya 5:31; Malaki 2:8, 9) M’nthaŵi ya ulamuliro wa Girisi, ansembe ambiri anagonjera Agirikiwo pankhani zachipembedzo. M’zaka za zana lachiŵiri B.C.E., Afarisi—gulu latsopano m’Chiyuda limene silinali kukhulupirira ansembe—linayamba kukhazikitsa miyambo mwa imene munthu wamba anatha kudziona kukhala woyera mofanana ndi wansembe. Miyambo imeneyi inawakopa ambiri, koma inali yowonjeza ku Chilamulo komanso yosavomerezeka.—Deuteronomo 4:2; 12:32 (13:1 m’makope achiyuda).
Afarisi anakhala akatswiri atsopano a Chilamulo, akumachita ntchito imene anaona kuti ansembe sakuichita. Popeza kuti Chilamulo cha Mose sichinawapatsepo ulamuliro, iwo anapanga njira zatsopano zomasulirira Malemba mwa mafotokozedwe osokoneza ndi mwa njira zina zimene mwachionekere zinali kuchirikiza malingaliro awo.a Pokhala oyang’anira ndi ochirikiza aakulu a miyambo imeneyi, iwo anapanga gulu lina laulamuliro mu Israyeli. Podzafika m’zaka za zana loyamba C.E., Afarisi anali atakhala amphamvu koposa m’Chiyuda.
Pamene anali kusonkhanitsa miyambo ya pakamwa imene inalipo ndi kufufuza zifukwa za m’Malemba kuti akhazikitse miyambo yawo inanso, Afarisi anaona kuti zochita zawo ziyenera kukhala ndi ulamuliro wowonjezeka. Lingaliro latsopano la chiyambi cha miyambo imeneyi linabadwa. Arabi anayamba kuphunzitsa kuti: “Mose analandira Torah ku Sinai ndi kumpatsira Yoswa, Yoswa anaipereka kwa akulu, ndipo akulu kwa aneneri. Ndipo aneneri anaipereka kwa amuna a msonkhano waukulu.”—Avot 1:1, Mishnah.
Ponena kuti, “Mose analandira Torah,” arabi sanali kungonena malamulo olembedwa komanso miyambo yawo yonse ya pakamwa. Iwo ankanena kuti miyambo imeneyi—yopangidwa ndi anthu—ndi Mulungu amene anampatsa Mose ku Sinai. Ndipo anaphunzitsa kuti Mulungu sanasiyire anthu kuti aikemo zimene munalibe, koma anafotokoza pakamwa zimene Chilamulo cholembedwa sichinanene. Malinga ndi kunena kwawo, Mose anapatsira mibadwo yotsatira chilamulo cha pakamwa chimenechi, osati kwa ansembe, koma kwa atsogoleri ena. Afarisi iwo eni ankanena kuti ndiwo oloŵa mzere “wopitirizabe” umenewu wa ulamuliro.
-