Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • Kuvumbulidwa ndi Mafanizo a Munda Wampesa
    Nsanja ya Olonda—1990 | January 1
    • “Munthu anali nawo ana aŵiri,” Yesu akusimba tero. “Nadza iye kwa woyamba nati, Mwanawe, kagwire lero ntchito ku munda wampesa. [Poyankha uyu adati, ‘ndidzatero, Mbuyanga,’ koma sanapite, NW]. Ndipo anadza kwa winayo, natero momwemo. Ndipo [poyankha uyu adati, ‘sindidzapita.’ Pambuyo pake analapa napita, NW]. Ndani wa aŵiriwo anachita chifuniro cha atate wake?” Yesu akufunsa tero.

  • Kuvumbulidwa ndi Mafanizo a Munda Wampesa
    Nsanja ya Olonda—1990 | January 1
    • Chotero Yesu akulongosola kuti: “Indetu ndinena kwa inu, kuti amisonkho ndi akazi achiŵereŵere amatsogolera inu, kuloŵa Ufumu wa [Mulungu, NW].” Kwenikwenidi, amisonkho ndi akazi achiŵereŵere poyambapo anakana kutumikira Mulungu. Koma kenaka, mofanana ndi mwana wachiŵiriyo, analapa ndipo anamtumikira. Kumbali ina, atsogoleri achipembedzo, mofanana ndi mwana woyamba, anadzinenera kutumikira Mulungu, komabe, monga mmene Yesu akudziŵitsira: “Yohane [Mbatizi] anadza kwa inu m’njira ya chilungamo, ndipo simunamvera iye; koma amisonkho ndi akazi achiŵereŵere anam’mvera iye; ndipo inu, mmene munachiwona, simulapa pambuyo pake, kuti mumvere iye.”

Mabuku a Chichewa (1974-2025)
Tulukani
Lowani
  • Chichewa
  • Tumizirani Ena
  • Zimene Mumakonda
  • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
  • Zoyenera Kutsatira
  • Nkhani Yosunga Chinsinsi
  • Privacy Settings
  • JW.ORG
  • Lowani
Tumizirani Ena