-
“Kodi Nchiyani Chidzakhala Chizindikiro cha Kukhalapo Kwanu”?Nsanja ya Olonda—1994 | February 15
-
-
13. Kodi nchifukwa ninji Akristu anakhoza kulabadira chenjezo la Yesu la kuthaŵa?
13 Koma, ngati Aromawo anali atachoka ku Yerusalemu, kodi nchifukwa ninji aliyense anafunikira kuthaŵa? Mawu a Yesu anasonyeza kuti zimene zinachitikazo zinali umboni wakuti ‘chipululutso cha Yerusalemu chinayandikira.’ (Luka 21:20) Inde, chipululutso. Iye ananeneratu za ‘chisautso chachikulu chonga chimene sichinayambe chakhalako kuyambira pachiyambi ndipo sichikakhalanso.’ Pafupifupi zaka zitatu ndi theka pambuyo pake, mu 70 C.E., Yerusalemu anakumanadi ndi ‘chisautso chachikulu’ chochokera kumagulu ankhondo Achiroma otsogozedwa ndi Kazembe Titus. (Mateyu 24:21; Marko 13:19) Koma, kodi nchifukwa ninji Yesu analongosola chimenechi kukhala chisautso chachikulu kuposa chilichonse chimene chinachitikapo pasadakhale kapena kufikira lerolino?
14. Kodi nchifukwa ninji tinganene kuti chimene chinachitikira Yerusalemu mu 70 C.E. chinali ‘chisautso chachikulu’ chimene sichinachitikepo kalelo ndi pambuyo pake?
14 Yerusalemu anasakazidwapo ndi Ababulo mu 607 B.C.E., ndipo mzindawo waona nkhondo zowopsa m’zaka za zana lathu lino. Komabe, chimene chinachitika mu 70 C.E. chinalidi chisautso chachikulu choposa china chilichonse. M’kulimbana kwa pafupifupi miyezi isanu, ankhondo a Titus anagonjetsa Ayuda. Anapha anthu pafupifupi 1,100,000 ndi kutenga undende pafupifupi 100,000. Ndiponso, Aroma anapasula Yerusalemu. Zimenezi zinapereka umboni wakuti dongosolo Lachiyuda la kulambira kumene kale kunali kovomerezedwa kozikidwa pakachisi linali litatheratu. (Ahebri 1:2) Inde, zochitika za mu 70 C.E. moyenerera zingalingaliridwe kukhala ‘chisautso chonga chimene sichinachitikepo [pamzindawo, mtundu, ndi dongosolo] kuyambira chiyambi cha dziko, kufikira tsopano, inde ndipo sichidzakhalanso.’—Mateyu 24:21.d
-
-
“Kodi Nchiyani Chidzakhala Chizindikiro cha Kukhalapo Kwanu”?Nsanja ya Olonda—1994 | February 15
-
-
d Mlembi wa ku Britain Matthew Henry anathirira ndemanga kuti: “Kuwonongedwa kwa Yerusalemu kochitidwa ndi Akasidi kunali koipa kwambiri, koma kotsiriziraku kunapambana. Kunapereka chiwopsezo cha kuphedwa kwa . . . Ayuda onse.”
-
-
“Kodi Nchiyani Chidzakhala Chizindikiro cha Kukhalapo Kwanu”?Nsanja ya Olonda—1994 | February 15
-
-
[Chithunzi patsamba 10]
Chisautso cha mu 70 C.E. pa Yerusalemu ndi dongosolo Lachiyuda chinali chachikulu koposa
-