-
‘Pitani Mukaphunzitse Anthu Kuti Akhale Ophunzira Anga’Nsanja ya Olonda (Yophunzira)—2020 | January
-
-
1-2. Kodi mngelo anauza azimayi ena kuti chiyani, nanga Yesu anawauza kuti chiyani?
M’MAWA wa pa Nisani 16 mu 33 C.E., azimayi ena oopa Mulungu anapita kumanda amene anaikamo thupi la Yesu Khristu. Limeneli linali tsiku lachiwiri chiikireni thupilo m’manda. Pa nthawiyi anali ndi chisoni ndipo anapita kuti akapake thupilo zonunkhiritsa. Koma atafika anadabwa kuona kuti m’mandamo munalibe thupi la Yesu. Ndiyeno mngelo ananena kuti Yesu wauka ndipo anawauza kuti: “Watsogola kupita ku Galileya. Kumeneko mukamuona.”—Mat. 28:1-7; Luka 23:56; 24:10.
-
-
‘Pitani Mukaphunzitse Anthu Kuti Akhale Ophunzira Anga’Nsanja ya Olonda (Yophunzira)—2020 | January
-
-
4 Yesu amafuna kuti otsatira ake onse azilalikira. Lamuloli sanalipereke kwa atumwi ake okhulupirika 11 okha. Tikutero chifukwa chakuti pa nthawi imene Yesu ankapereka lamuloli paphiri lina la ku Galileya panalinso anthu ena osati atumwi okha. Paja mngelo anawauza azimayi aja kuti: “Mukamuona [ku Galileya].” Zimenezi zikusonyeza kuti azimayi okhulupirika analiponso pamsonkhanowo. Komanso mtumwi Paulo ananena kuti Yesu “anaonekeranso kwa abale oposa 500 pa nthawi imodzi.” (1 Akor. 15:6) Kodi zimenezi zinachitika kuti?
-