Watchtower LAIBULALE YA PA INTANETI
Watchtower
LAIBULALE YA PA INTANETI
Chichewa
  • BAIBULO
  • MABUKU
  • MISONKHANO
  • w98 1/1 tsamba 29
  • ‘Pangani Ophunzira mwa Anthu a Mitundu Yonse’

Palibe Vidiyo.

Pepani vidiyoyi ikukanika kutsegula.

  • ‘Pangani Ophunzira mwa Anthu a Mitundu Yonse’
  • Nsanja ya Olonda—1998
Nsanja ya Olonda—1998
w98 1/1 tsamba 29

‘Pangani Ophunzira mwa Anthu a Mitundu Yonse’

“CHIFUKWA chake mukani nimupange ophunzira mwa anthu a mitundu yonse, kuwabatiza iwo m’dzina la Atate ndi la Mwana ndi la Mzimu Woyera.” Umu ndimo mmene Baibulo la New World Translation linatembenuzira lamulo la Yesu pa Mateyu 28:19. Komabe, kutembenuza kumeneku ena akutsutsa. Mwachitsanzo, kabuku kena kachipembedzo kanati: “Lemba lachigiriki limeneli lingamveke bwino kokha ngati litatembenuzidwa motere: ‘Pangani ophunzira mwa mitundu yonse.’” Kodi zimenezo nzoona?

Mabaibulo ambiri anatembenuzadi choncho kuti, “Pangani ophunzira mwa mitundu yonse,” ndipo kumeneko kunali kutembenuza mwachindunji mawu achigiriki. Choncho, kodi pali chifukwa chotani choŵerengera kuti, “Pangani ophunzira mwa anthu a mitundu yonse, ndi kuwabatiza”? Chifukwa cha nkhani yakeyo. Mawu akuti “kuwabatiza” kwenikweni akutanthauza anthu, osati mitundu. Katswiri wazamaphunziro wa ku Germany, Hans Bruns, anati: “[mawu] akuti ‘iwo’ sakutanthauza mitundu (Chigiriki chimasiyanitsa bwino), koma anthu a m’mitunduyo.”

Ndiponso, tiyenera kulingalira mmene anthu anatsatira lamulo la Yesu limenelo. Ponena za utumiki wa Paulo ndi Barnaba ku Derbe, mzinda wa ku Asia Minor, timaŵerenga kuti: “Pamene analalikira Uthenga Wabwino pamudzipo, nayesa ambiri akuphunzira [napeza ophunzira oŵerengeka, NW], anabwera ku Lustra ndi Ikoniya ndi Antiokeya.” (Machitidwe 14:21) Taonani kuti Paulo ndi Barnaba sanapange onse mumzinda wa Derbe kukhala ophunzira, koma kuti ena mwa anthu a ku Derbe.

Mofananamo, ponena za nthaŵi ya mapeto, buku la Chivumbulutso linaneneratu kuti si mitundu yonse yomwe idzatumikira Mulungu, koma ‘khamu lalikulu . . . ochokera mwa mtundu uliwonse ndi mafuko ndi anthu ndi manenedwe,’ ndiwo adzamtumikira. (Chivumbulutso 7:9) Choncho, tikuchirikiza Baibulo la New World Translation kuti nlodalirika chifukwa linatembenuza bwino ‘Lemba lililonse, limene adaliuzira Mulungu.’​—2 Timoteo 3:16.

    Mabuku a Chichewa (1974-2025)
    Tulukani
    Lowani
    • Chichewa
    • Tumizirani Ena
    • Zimene Mumakonda
    • Copyright © 2025 Watch Tower Bible and Tract Society of Pennsylvania
    • Zoyenera Kutsatira
    • Nkhani Yosunga Chinsinsi
    • Privacy Settings
    • JW.ORG
    • Lowani
    Tumizirani Ena