-
Kodi Mumagwiritsa Ntchito “Nzeru Yochokera Kumwamba” pa Moyo Wanu?Yandikirani Yehova
-
-
11 Kodi mungatani ngati mwazindikira kuti mwakhumudwitsa Mkhristu mnzanu? Yesu anati: “Ngati wabweretsa mphatso yako paguwa lansembe, ndipo uli pomwepo wakumbukira kuti m’bale wako ali nawe chifukwa, siya mphatso yako patsogolo pa guwa lansembe pomwepo n’kuchokapo. Choyamba pita ukakhazikitse mtendere ndi m’bale wakoyo. Kenako ukabwerenso n’kudzapereka mphatso yakoyo.” (Mateyu 5:23, 24) Muziyamba ndi inuyo kupita kukakambirana ndi m’bale wanuyo ndipo mukamatero mumasonyeza kuti mukutsatira malangizo amenewa. Kodi cholinga chanu chiyenera kukhala chiyani? ‘Kukakhazikitsa mtendere.’b Kuti zimenezi zitheke mungafunike kuvomereza, osati kukana, kuti nkhaniyo yamukhumudwitsa mnzanuyo. Ngati pa nthawi yonse imene mukulankhulana mutakhala ndi cholinga choti mubwezeretse mtendere, mukhoza kuthetsa kusamvana, kupepesana ndiponso kukhululukirana. Mukayesetsa kuti mukhazikitse mtendere, mumasonyeza kuti mukutsogoleredwa ndi nzeru za Mulungu.
-
-
Kodi Mumagwiritsa Ntchito “Nzeru Yochokera Kumwamba” pa Moyo Wanu?Yandikirani Yehova
-
-
b Mawu a Chigiriki amene anawamasulira kuti “ukakhazikitse mtendere,” amatanthauza “kusiya kukhala adani n’kukhala mabwenzi, kugwirizananso ndiponso kuyambiranso kuchitira zinthu limodzi.” Choncho cholinga chanu n’kuthandiza m’bale wanu amene wakhumudwayo kuti ngati zingatheke asiye kukhumudwa nanu.—Aroma 12:18.
-