-
Chilungamo Osati Miyambo YapakamwaNsanja ya Olonda—1990 | October 1
-
-
12. (a) Kodi nkusintha kotani kuchoka pa njira yanthaŵi zonseyi ya kupereka zilozero ku Malemba Achihebri kumene Yesu anakupanga mu Ulaliki wake wa pa Phiri, ndipo kodi nchifukwa ninji? (b) Kodi tikuphunziranji m’kugwiritsira ntchito kwachisanu ndi chimodzi kwa mawu akuti “Kunanenedwa”?
12 Pamene Yesu poyambirira anagwira mawu kuchokera m’Malemba Achihebri, iye anati: “Kwalembedwa.” (Mateyu 4:4, 7, 10) Koma nthaŵi zisanu ndi imodzi mu Ulaliki wa pa Phiri, iye anayamba yomwe inamveka ngati ndemanga yochokera m’Malemba Achihebri ndi mawu akuti: “Kunanenedwa.” (Mateyu 5:21, 27, 31, 33, 38, 43) Kodi nchifukwa ninji? Chifukwa chakuti iye ankalozera ku Malemba monga momwe anamasulidwira mlingaliro la miyambo ya Afarisi imene inatsutsana ndi malamulo a Mulungu. (Deuteronomo 4:2; Mateyu 15:3) Ichi chamveketsedwa m’kulozera kwa Yesu kwa chisanu ndi chimodzi ndi komalizira uku mumpambowu: “Munamva kuti kunanenedwa, Uzikondana ndi mnansi wako, ndi kumuda mdani wako.” Koma panalibe lamulo la Mose limene linati, ‘Uzida mdani wako.’ Alembi ndi Afarisi ndiwo analinena. Uku kunali kumasulira kwawo Chilamulo kwa kukondana ndi mnansi wako—mnansi wako Wachiyuda, osati wina aliyense.
-
-
Chilungamo Osati Miyambo YapakamwaNsanja ya Olonda—1990 | October 1
-
-
16. Kodi ndi kachitidwe kotani Kachiyuda kamene kanapangitsa kulumbira kukhala kopanda pake, ndipo kodi ndi kaimidwe kotani kamene Yesu anatenga?
16 M’lingaliro lofanana ndi ili, Yesu anapitiriza motere: ‘Ndiponso, munamva kuti kunanenedwa kwa iwo akale, Usalumbire [popanda kukwaniritsa, NW] . . . koma ine ndinena kwa inu, Musalumbire konse.’ Panthaŵiyi Ayuda ankagwiritsira ntchito molakwa malumbiro ndipo ankapereka malumbiro ambiri pa zinthu zazing’ono popanda kuzikwaniritsa. Koma Yesu anati: ‘Musalumbire konse . . . Koma manenedwe anu akhale Inde, inde; Iai, iai.’ Lamulo lake linali lopepuka: Khalani wonena zowonadi nthaŵi zonse, osafunikira kutsimikizira mawu anu ndi lumbiro. Kulumbira kusiireni kunkhani zina.—Mateyu 5:33-37; yerekezerani ndi 23:16-22.
-