-
Chilungamo Osati Miyambo YapakamwaNsanja ya Olonda—1990 | October 1
-
-
16. Kodi ndi kachitidwe kotani Kachiyuda kamene kanapangitsa kulumbira kukhala kopanda pake, ndipo kodi ndi kaimidwe kotani kamene Yesu anatenga?
16 M’lingaliro lofanana ndi ili, Yesu anapitiriza motere: ‘Ndiponso, munamva kuti kunanenedwa kwa iwo akale, Usalumbire [popanda kukwaniritsa, NW] . . . koma ine ndinena kwa inu, Musalumbire konse.’ Panthaŵiyi Ayuda ankagwiritsira ntchito molakwa malumbiro ndipo ankapereka malumbiro ambiri pa zinthu zazing’ono popanda kuzikwaniritsa. Koma Yesu anati: ‘Musalumbire konse . . . Koma manenedwe anu akhale Inde, inde; Iai, iai.’ Lamulo lake linali lopepuka: Khalani wonena zowonadi nthaŵi zonse, osafunikira kutsimikizira mawu anu ndi lumbiro. Kulumbira kusiireni kunkhani zina.—Mateyu 5:33-37; yerekezerani ndi 23:16-22.
-
-
Chilungamo Osati Miyambo YapakamwaNsanja ya Olonda—1990 | October 1
-
-
20. Mmalo mwa kuchotsapo Chilamulo cha Mose, kodi ndimotani mmene Yesu anakulitsira ndi kuzamitsa mphamvu yake ndikuchikweza?
20 Chotero pamene Yesu analozera ku mbali za Chilamulo ndikuwonjezera kuti, “Koma Ine ndinena kwa inu,” sanali kuchotsa Chilamulo cha Mose ndikuchilowa mmalo ndi chinachake. Ayi, koma anali kuzamitsa ndi kukulitsa mphamvu yake mwa kusonyeza mzimu wokhala kumbuyo kwake. Chilamulo chapamwamba chaubale chimapereka chiweruzo chakuti wopitiriza kukhala ndi chidani ngwakupha. Chilamulo chapamwamba cha chiyero chimatsutsa kuti kupitiriza nawo maganizo okhumbira ndiko chigololo. Chilamulo chapamwamba chaukwati chimaletsa kusudzulana kwachinyengo kuti ndiko njira yotsogolera ku kukwatirananso kwachigololo. Chilamulo chapamwamba cha chowonadi chimasonyeza kuti kulapa kobwerezabwereza nkosayenera. Chilamulo chapamwamba cha kudekha chimaletsa kubwezera. Chilamulo chapamwamba cha chikondi chimafuna chikondi chaumulungu chomwe chiribe polekezera.
-